< Masalimo 3 >
1 Salimo la Davide. Atathawa mwana wake Abisalomu. Inu Yehova, achulukadi adani anga! Achulukadi amene andiwukira!
Psaume de David. A l’occasion de sa fuite devant Absalom, son fils. O Éternel, que mes ennemis sont nombreux! Quelle multitude se lève contre moi!
2 Ambiri akunena za ine kuti, “Mulungu sadzamupulumutsa.” (Sela)
Combien qui disent à mon sujet: Plus de salut pour lui auprès de Dieu! (Pause)
3 Koma Inu Yehova, ndinu chishango chonditeteza, Inu mwandiveka ulemerero ndipo mwanditukula.
Mais toi, ô Éternel! Tu es mon bouclier, Tu es ma gloire, et tu relèves ma tête.
4 Kwa Yehova, Ine ndilira mofuwula ndipo Iye amandiyankha kuchokera ku phiri lake loyera. (Sela)
De ma voix je crie à l’Éternel, Et il me répond de sa montagne sainte. (Pause)
5 Ine ndimagona ndi kupeza tulo; ndimadzukanso chifukwa Yehova amandichirikiza.
Je me couche, et je m’endors; Je me réveille, car l’Éternel est mon soutien.
6 Sindidzaopa adani anga osawerengeka amene abwera kulimbana nane kuchokera ku madera onse.
Je ne crains pas les myriades de peuples Qui m’assiègent de toutes parts.
7 Dzukani, Inu Yehova! Pulumutseni, Inu Mulungu wanga. Akantheni adani anga onse pa msagwada; gululani mano a anthu oyipa.
Lève-toi, Éternel! Sauve-moi, mon Dieu! Car tu frappes à la joue tous mes ennemis, Tu brises les dents des méchants.
8 Chipulumutso chimachokera kwa Yehova. Madalitso akhale pa anthu anu. (Sela)
Le salut est auprès de l’Éternel: Que ta bénédiction soit sur ton peuple! (Pause)