< Masalimo 3 >

1 Salimo la Davide. Atathawa mwana wake Abisalomu. Inu Yehova, achulukadi adani anga! Achulukadi amene andiwukira!
A Psalm of David, in his fleeing from the face of Absalom his son. Jehovah, how have my distresses multiplied! Many are rising up against me.
2 Ambiri akunena za ine kuti, “Mulungu sadzamupulumutsa.” (Sela)
Many are saying of my soul, 'There is no salvation for him in God.' (Selah)
3 Koma Inu Yehova, ndinu chishango chonditeteza, Inu mwandiveka ulemerero ndipo mwanditukula.
And Thou, O Jehovah, [art] a shield for me, My honour, and lifter up of my head.
4 Kwa Yehova, Ine ndilira mofuwula ndipo Iye amandiyankha kuchokera ku phiri lake loyera. (Sela)
My voice [is] unto Jehovah: I call: And He answereth me from his holy hill, (Selah)
5 Ine ndimagona ndi kupeza tulo; ndimadzukanso chifukwa Yehova amandichirikiza.
I — I have lain down, and I sleep, I have waked, for Jehovah sustaineth me.
6 Sindidzaopa adani anga osawerengeka amene abwera kulimbana nane kuchokera ku madera onse.
I am not afraid of myriads of people, That round about they have set against me.
7 Dzukani, Inu Yehova! Pulumutseni, Inu Mulungu wanga. Akantheni adani anga onse pa msagwada; gululani mano a anthu oyipa.
Rise, O Jehovah! save me, my God. Because Thou hast smitten All mine enemies [on] the cheek. The teeth of the wicked Thou hast broken.
8 Chipulumutso chimachokera kwa Yehova. Madalitso akhale pa anthu anu. (Sela)
Of Jehovah [is] this salvation; On Thy people [is] Thy blessing! (Selah)

< Masalimo 3 >