< Masalimo 3 >

1 Salimo la Davide. Atathawa mwana wake Abisalomu. Inu Yehova, achulukadi adani anga! Achulukadi amene andiwukira!
A psalm of David when fled he from before - Absalom son his. O Yahweh how! they are many opponents my many [people] [are] rising up on me.
2 Ambiri akunena za ine kuti, “Mulungu sadzamupulumutsa.” (Sela)
Many [people] [are] saying of self my there not [is] deliverance for him in God (Selah)
3 Koma Inu Yehova, ndinu chishango chonditeteza, Inu mwandiveka ulemerero ndipo mwanditukula.
And you O Yahweh [are] a shield behind me honor my and [the one who] lifts up head my.
4 Kwa Yehova, Ine ndilira mofuwula ndipo Iye amandiyankha kuchokera ku phiri lake loyera. (Sela)
Voice my to Yahweh I called out and he answered me from [the] mountain of holiness his (Selah)
5 Ine ndimagona ndi kupeza tulo; ndimadzukanso chifukwa Yehova amandichirikiza.
I I lay down and I slept! I awoke for Yahweh he sustains me.
6 Sindidzaopa adani anga osawerengeka amene abwera kulimbana nane kuchokera ku madera onse.
Not I will be afraid from ten thousands of people who all around they have taken a stand on me.
7 Dzukani, Inu Yehova! Pulumutseni, Inu Mulungu wanga. Akantheni adani anga onse pa msagwada; gululani mano a anthu oyipa.
Arise! O Yahweh - save me O God my for you have struck all enemies my jaw [the] teeth of wicked [people] you have broken.
8 Chipulumutso chimachokera kwa Yehova. Madalitso akhale pa anthu anu. (Sela)
[belongs] to Yahweh deliverance [is] towards people your blessing your (Selah)

< Masalimo 3 >