< Masalimo 3 >

1 Salimo la Davide. Atathawa mwana wake Abisalomu. Inu Yehova, achulukadi adani anga! Achulukadi amene andiwukira!
“A psalm of David, when he fled from before Abshalom his son.” Lord, how numerous are my assailants! how many, that rise up against me!
2 Ambiri akunena za ine kuti, “Mulungu sadzamupulumutsa.” (Sela)
Many say of my soul, There is no help for him with God. (Selah)
3 Koma Inu Yehova, ndinu chishango chonditeteza, Inu mwandiveka ulemerero ndipo mwanditukula.
But thou, O Lord, art a shield around me, my glory, and he that lifteth up my head.
4 Kwa Yehova, Ine ndilira mofuwula ndipo Iye amandiyankha kuchokera ku phiri lake loyera. (Sela)
With my voice I call unto the Lord, and he answereth me out of his holy mountain. (Selah)
5 Ine ndimagona ndi kupeza tulo; ndimadzukanso chifukwa Yehova amandichirikiza.
I laid myself down and slept: I awoke; for the Lord sustaineth me.
6 Sindidzaopa adani anga osawerengeka amene abwera kulimbana nane kuchokera ku madera onse.
I will not be afraid of ten thousands of people, that have placed themselves round about against me.
7 Dzukani, Inu Yehova! Pulumutseni, Inu Mulungu wanga. Akantheni adani anga onse pa msagwada; gululani mano a anthu oyipa.
Arise, O Lord, help me, O my God; for thou smitest all my enemies upon the cheek bone: the teeth of the wicked dost thou break.
8 Chipulumutso chimachokera kwa Yehova. Madalitso akhale pa anthu anu. (Sela)
Salvation belongeth unto the Lord: thy blessing be upon thy people. (Selah)

< Masalimo 3 >