< Masalimo 29 >
1 Salimo la Davide. Perekani kwa Yehova, inu anthu amphamvu, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
En psalm av David. Given åt HERREN, I Guds sönder, given åt HERREN ära och makt;
2 Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake, pembedzani Yehova mwa kukongola kwa chiyero chake.
given åt HERREN hans namns ära, tillbedjen HERREN i helig skrud.
3 Liwu la Yehova lili pamwamba pa madzi; Mulungu waulemerero abangula, Yehova abangula pamwamba pa madzi amphamvu.
HERRENS röst går ovan vattnen; Gud, den härlige, dundrar, ja, HERREN, ovan de stora vattnen.
4 Liwu la Yehova ndi lamphamvu; liwu la Yehova ndi laulemerero.
HERRENS röst ljuder med makt, HERRENS röst ljuder härligt.
5 Liwu la Yehova limathyola mikungudza; Yehova amathyolathyola mikungudza ya ku Lebanoni.
HERRENS röst bräcker cedrar, HERREN bräcker Libanons cedrar.
6 Iye amachititsa Lebanoni kulumphalumpha ngati mwana wangʼombe, Siriyoni ngati mwana wa njati:
Han kommer dem att hoppa likasom kalvar, Libanon och Sirjon såsom unga vildoxar.
7 Liwu la Yehova limakantha ngati kungʼanima kwa mphenzi.
HERRENS röst sprider ljungeldslågor.
8 Liwu la Yehova limagwedeza chipululu; Yehova amagwedeza chipululu cha Kadesi.
HERRENS röst kommer öknen att bäva, HERREN kommer Kades' öken att bäva.
9 Liwu la Yehova limapindapinda mibawa ndi kuyeretsa nkhalango. Ndipo mʼNyumba mwake onse amafuwula kuti, “Ulemerero!”
HERRENS röst bringar hindarna att föda; skogarnas klädnad rycker den bort. I hans himmelska boning förkunnar allting hans ära.
10 Yehova amakhala pamwamba pa madzi osefukira, Yehova ndiye mfumu kwamuyaya.
HERREN på sin tron bjöd floden komma, och HERREN tronar såsom konung evinnerligen.
11 Yehova amapereka mphamvu kwa anthu ake; Yehova amadalitsa anthu ake ndi mtendere.
HERREN skall giva makt åt sitt folk, HERREN skall välsigna sitt folk med frid.