< Masalimo 29 >

1 Salimo la Davide. Perekani kwa Yehova, inu anthu amphamvu, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
¡Tributen a Yavé, oh hijos de los poderosos! ¡Tributen a Yavé la gloria y el poder!
2 Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake, pembedzani Yehova mwa kukongola kwa chiyero chake.
¡Tributen a Yavé la gloria debida a su Nombre! ¡Póstrense ante Yavé en el esplendor de la santidad!
3 Liwu la Yehova lili pamwamba pa madzi; Mulungu waulemerero abangula, Yehova abangula pamwamba pa madzi amphamvu.
Voz de Yavé sobre las aguas: ¡El ʼElohim de gloria truena! ¡Yavé está sobre muchas aguas!
4 Liwu la Yehova ndi lamphamvu; liwu la Yehova ndi laulemerero.
Voz de Yavé es poderosa, Voz de Yavé es majestuosa.
5 Liwu la Yehova limathyola mikungudza; Yehova amathyolathyola mikungudza ya ku Lebanoni.
Voz de Yavé que quiebra los cedros, Yavé destroza los cedros del Líbano.
6 Iye amachititsa Lebanoni kulumphalumpha ngati mwana wangʼombe, Siriyoni ngati mwana wa njati:
Él hace saltar al Líbano como un becerro.
7 Liwu la Yehova limakantha ngati kungʼanima kwa mphenzi.
Voz de Yavé que enciende llamaradas.
8 Liwu la Yehova limagwedeza chipululu; Yehova amagwedeza chipululu cha Kadesi.
Voz de Yavé que estremece el desierto. Yavé sacude al desierto de Cades.
9 Liwu la Yehova limapindapinda mibawa ndi kuyeretsa nkhalango. Ndipo mʼNyumba mwake onse amafuwula kuti, “Ulemerero!”
Voz de Yavé que estremece los robles y desnuda los bosques. En su Templo todos proclaman su gloria.
10 Yehova amakhala pamwamba pa madzi osefukira, Yehova ndiye mfumu kwamuyaya.
Yavé preside en el diluvio. Yavé se sienta como Rey para siempre.
11 Yehova amapereka mphamvu kwa anthu ake; Yehova amadalitsa anthu ake ndi mtendere.
Yavé dará fortaleza a su pueblo. Yavé bendecirá a su pueblo con paz.

< Masalimo 29 >