< Masalimo 29 >

1 Salimo la Davide. Perekani kwa Yehova, inu anthu amphamvu, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
مزمور داوود. ای فرشتگان، خداوند را ستایش کنید! شکوه و عظمت او را بستایید!
2 Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake, pembedzani Yehova mwa kukongola kwa chiyero chake.
خداوند را به خاطر جلال نامش بپرستید. خداوند را در شکوه قدوسیتش پرستش کنید.
3 Liwu la Yehova lili pamwamba pa madzi; Mulungu waulemerero abangula, Yehova abangula pamwamba pa madzi amphamvu.
صدای خداوند از فراز دریاها شنیده می‌شود؛ او همچون رعد می‌غرد! صدای او بر اقیانوسها طنین‌افکن است!
4 Liwu la Yehova ndi lamphamvu; liwu la Yehova ndi laulemerero.
صدای خداوند پرقدرت و باشکوه است.
5 Liwu la Yehova limathyola mikungudza; Yehova amathyolathyola mikungudza ya ku Lebanoni.
صدای خداوند درختان سِدر را می‌شکند. خداوند درختان سِدر لبنان را خُرد می‌کند.
6 Iye amachititsa Lebanoni kulumphalumpha ngati mwana wangʼombe, Siriyoni ngati mwana wa njati:
او کوههای لبنان را می‌لرزاند و کوه حرمون را مانند گوساله به جست و خیز وا می‌دارد.
7 Liwu la Yehova limakantha ngati kungʼanima kwa mphenzi.
صدای خداوند رعد و برق ایجاد می‌کند،
8 Liwu la Yehova limagwedeza chipululu; Yehova amagwedeza chipululu cha Kadesi.
دشتها را به لرزه در می‌آورد و صحرای قادش را می‌جنباند.
9 Liwu la Yehova limapindapinda mibawa ndi kuyeretsa nkhalango. Ndipo mʼNyumba mwake onse amafuwula kuti, “Ulemerero!”
صدای خداوند درخت بلوط را می‌لرزاند و برگهای درختان جنگل را به زمین می‌ریزد. در خانهٔ خداوند، همه جلال و عظمت او را می‌ستایند.
10 Yehova amakhala pamwamba pa madzi osefukira, Yehova ndiye mfumu kwamuyaya.
خداوند بر آبهای عمیق فرمان می‌راند و تا به ابد سلطنت می‌نماید.
11 Yehova amapereka mphamvu kwa anthu ake; Yehova amadalitsa anthu ake ndi mtendere.
خداوند به قوم برگزیدهٔ خود قدرت می‌بخشد و صلح و سلامتی نصیب ایشان می‌کند.

< Masalimo 29 >