< Masalimo 29 >

1 Salimo la Davide. Perekani kwa Yehova, inu anthu amphamvu, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
مزمور داود ای فرزندان خدا، خداوند را توصیف کنید. جلال و قوت را برای خداوندتوصیف نمایید.۱
2 Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake, pembedzani Yehova mwa kukongola kwa chiyero chake.
خداوند را به جلال اسم اوتمجید نمایید. خداوند را در زینت قدوسیت سجده کنید.۲
3 Liwu la Yehova lili pamwamba pa madzi; Mulungu waulemerero abangula, Yehova abangula pamwamba pa madzi amphamvu.
آواز خداوند فوق آبها است. خدای جلال رعد می‌دهد. خداوند بالای آبهای بسیار است.۳
4 Liwu la Yehova ndi lamphamvu; liwu la Yehova ndi laulemerero.
آواز خداوند با قوت است. آوازخداوند با جلال است.۴
5 Liwu la Yehova limathyola mikungudza; Yehova amathyolathyola mikungudza ya ku Lebanoni.
آواز خداوند سروهای آزاد را می‌شکند. خداوند سروهای آزاد لبنان رامی شکند.۵
6 Iye amachititsa Lebanoni kulumphalumpha ngati mwana wangʼombe, Siriyoni ngati mwana wa njati:
آنها را مثل گوساله می‌جهاند. لبنان وسریون را مثل بچه گاو وحشی.۶
7 Liwu la Yehova limakantha ngati kungʼanima kwa mphenzi.
آواز خداوندزبانه های آتش را می‌شکافد.۷
8 Liwu la Yehova limagwedeza chipululu; Yehova amagwedeza chipululu cha Kadesi.
آواز خداوندصحرا را متزلزل می‌سازد. خداوند صحرای قادش را متزلزل می‌سازد.۸
9 Liwu la Yehova limapindapinda mibawa ndi kuyeretsa nkhalango. Ndipo mʼNyumba mwake onse amafuwula kuti, “Ulemerero!”
آواز خداوند غزالهارا به درد زه می‌اندازد، و جنگل را بی‌برگ می‌گرداند. و در هیکل او جمیع جلال را ذکرمی کنند.۹
10 Yehova amakhala pamwamba pa madzi osefukira, Yehova ndiye mfumu kwamuyaya.
خداوند بر طوفان جلوس نموده. خداوند نشسته است پادشاه تا ابدالاباد.۱۰
11 Yehova amapereka mphamvu kwa anthu ake; Yehova amadalitsa anthu ake ndi mtendere.
خداوند قوم خود را قوت خواهد بخشید. خداوند قوم خود را به سلامتی مبارک خواهدنمود.۱۱

< Masalimo 29 >