< Masalimo 29 >

1 Salimo la Davide. Perekani kwa Yehova, inu anthu amphamvu, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
Psalmus David, In consummatione tabernaculi. Afferte Domino filii Dei: afferte Domino filios arietum:
2 Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake, pembedzani Yehova mwa kukongola kwa chiyero chake.
Afferte Domino gloriam et honorem, afferte Domino gloriam nomini eius: adorate Dominum in atrio sancto eius.
3 Liwu la Yehova lili pamwamba pa madzi; Mulungu waulemerero abangula, Yehova abangula pamwamba pa madzi amphamvu.
Vox Domini super aquas, Deus maiestatis intonuit: Dominus super aquas multas.
4 Liwu la Yehova ndi lamphamvu; liwu la Yehova ndi laulemerero.
Vox Domini in virtute: vox Domini in magnificentia.
5 Liwu la Yehova limathyola mikungudza; Yehova amathyolathyola mikungudza ya ku Lebanoni.
Vox Domini confringentis cedros: et confringet Dominus cedros Libani:
6 Iye amachititsa Lebanoni kulumphalumpha ngati mwana wangʼombe, Siriyoni ngati mwana wa njati:
Et comminuet eas tamquam vitulum Libani: et dilectus quemadmodum filius unicornium.
7 Liwu la Yehova limakantha ngati kungʼanima kwa mphenzi.
Vox Domini intercidentis flammam ignis:
8 Liwu la Yehova limagwedeza chipululu; Yehova amagwedeza chipululu cha Kadesi.
vox Domini concutientis desertum: et commovebit Dominus desertum Cades.
9 Liwu la Yehova limapindapinda mibawa ndi kuyeretsa nkhalango. Ndipo mʼNyumba mwake onse amafuwula kuti, “Ulemerero!”
Vox Domini praeparantis cervos, et revelabit condensa: et in templo eius omnes dicent gloriam.
10 Yehova amakhala pamwamba pa madzi osefukira, Yehova ndiye mfumu kwamuyaya.
Dominus diluvium inhabitare facit: et sedebit Dominus rex in aeternum.
11 Yehova amapereka mphamvu kwa anthu ake; Yehova amadalitsa anthu ake ndi mtendere.
Dominus virtutem populo suo dabit: Dominus benedicet populo suo in pace.

< Masalimo 29 >