< Masalimo 29 >
1 Salimo la Davide. Perekani kwa Yehova, inu anthu amphamvu, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
Ein Psalm Davids. Bringet her dem HERRN, ihr Gewaltigen bringet her dem HERRN Ehre und Stärke!
2 Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake, pembedzani Yehova mwa kukongola kwa chiyero chake.
Bringet dem HERRN Ehre seines Namens; betet an den HERRN in heiligem Schmuck!
3 Liwu la Yehova lili pamwamba pa madzi; Mulungu waulemerero abangula, Yehova abangula pamwamba pa madzi amphamvu.
Die Stimme des HERRN gehet auf den Wassern; der Gott der Ehren donnert, der HERR auf großen Wassern.
4 Liwu la Yehova ndi lamphamvu; liwu la Yehova ndi laulemerero.
Die Stimme des HERRN gehet mit Macht; die Stimme des HERRN gehet herrlich.
5 Liwu la Yehova limathyola mikungudza; Yehova amathyolathyola mikungudza ya ku Lebanoni.
Die Stimme des HERRN zerbricht die Zedern; der HERR zerbricht die Zedern im Libanon
6 Iye amachititsa Lebanoni kulumphalumpha ngati mwana wangʼombe, Siriyoni ngati mwana wa njati:
und machet sie löcken wie ein Kalb, Libanon und Sirion wie ein junges Einhorn.
7 Liwu la Yehova limakantha ngati kungʼanima kwa mphenzi.
Die Stimme des HERRN häuet wie Feuerflammen.
8 Liwu la Yehova limagwedeza chipululu; Yehova amagwedeza chipululu cha Kadesi.
Die Stimme des HERRN erreget die Wüste; die Stimme des HERRN erreget die Wüste Kades.
9 Liwu la Yehova limapindapinda mibawa ndi kuyeretsa nkhalango. Ndipo mʼNyumba mwake onse amafuwula kuti, “Ulemerero!”
Die Stimme des HERRN erreget die Hindinnen und entblößet die Wälder. Und in seinem Tempel wird ihm jedermann Ehre sagen.
10 Yehova amakhala pamwamba pa madzi osefukira, Yehova ndiye mfumu kwamuyaya.
Der HERR sitzt, eine Sintflut anzurichten. Und der HERR bleibt ein König in Ewigkeit.
11 Yehova amapereka mphamvu kwa anthu ake; Yehova amadalitsa anthu ake ndi mtendere.
Der HERR wird seinem Volk Kraft geben; der HERR wird sein Volk segnen mit Frieden.