< Masalimo 29 >

1 Salimo la Davide. Perekani kwa Yehova, inu anthu amphamvu, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
Cantique de David. Fils de Dieu, rendez à l'Éternel, rendez à l'Éternel l'honneur et la gloire!
2 Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake, pembedzani Yehova mwa kukongola kwa chiyero chake.
Rendez à l'Éternel l'honneur dû à son nom! Adorez l'Éternel avec une pompe sainte!
3 Liwu la Yehova lili pamwamba pa madzi; Mulungu waulemerero abangula, Yehova abangula pamwamba pa madzi amphamvu.
La voix de l'Éternel retentit sur les eaux, le Dieu glorieux fait gronder le tonnerre; on entend l'Éternel sur les grandes eaux.
4 Liwu la Yehova ndi lamphamvu; liwu la Yehova ndi laulemerero.
La voix de l'Éternel est puissante, la voix de l'Éternel est majestueuse;
5 Liwu la Yehova limathyola mikungudza; Yehova amathyolathyola mikungudza ya ku Lebanoni.
la voix de l'Éternel brise les cèdres, l'Éternel brise les cèdres du Liban,
6 Iye amachititsa Lebanoni kulumphalumpha ngati mwana wangʼombe, Siriyoni ngati mwana wa njati:
et Il les fait bondir, comme les jeunes taureaux, et le Liban et le Sirion, comme les buffles.
7 Liwu la Yehova limakantha ngati kungʼanima kwa mphenzi.
La voix de l'Éternel darde des flammes de feu;
8 Liwu la Yehova limagwedeza chipululu; Yehova amagwedeza chipululu cha Kadesi.
la voix de l'Éternel ébranle le désert, l'Éternel ébranle le désert de Kadès.
9 Liwu la Yehova limapindapinda mibawa ndi kuyeretsa nkhalango. Ndipo mʼNyumba mwake onse amafuwula kuti, “Ulemerero!”
La voix de l'Éternel fait avorter les biches, elle dépouille les forêts; et dans Son palais tout s'écrie: Gloire!
10 Yehova amakhala pamwamba pa madzi osefukira, Yehova ndiye mfumu kwamuyaya.
L'Éternel sur son trône présidait au déluge, et sur son trône l'Éternel régnera à jamais.
11 Yehova amapereka mphamvu kwa anthu ake; Yehova amadalitsa anthu ake ndi mtendere.
L'Éternel donnera la force à son peuple; l'Éternel bénira son peuple de la paix.

< Masalimo 29 >