< Masalimo 29 >
1 Salimo la Davide. Perekani kwa Yehova, inu anthu amphamvu, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
Psalmo de David. Tributu al la Eternulo, vi potenculoj, Tributu al la Eternulo honoron kaj forton.
2 Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake, pembedzani Yehova mwa kukongola kwa chiyero chake.
Tributu al la Eternulo la honoron de Lia nomo; Kliniĝu antaŭ la Eternulo en sankta ornamo.
3 Liwu la Yehova lili pamwamba pa madzi; Mulungu waulemerero abangula, Yehova abangula pamwamba pa madzi amphamvu.
La voĉo de la Eternulo iras super la akvoj; La Dio de gloro tondras, La Eternulo super grandaj akvoj.
4 Liwu la Yehova ndi lamphamvu; liwu la Yehova ndi laulemerero.
La voĉo de la Eternulo iras kun forto, La voĉo de la Eternulo iras kun majesto.
5 Liwu la Yehova limathyola mikungudza; Yehova amathyolathyola mikungudza ya ku Lebanoni.
La voĉo de la Eternulo rompas cedrojn, La Eternulo rompas la cedrojn de Lebanon.
6 Iye amachititsa Lebanoni kulumphalumpha ngati mwana wangʼombe, Siriyoni ngati mwana wa njati:
Li saltigas ilin kiel bovidon, Lebanonon kaj Sirjonon kiel bubalidon.
7 Liwu la Yehova limakantha ngati kungʼanima kwa mphenzi.
La voĉo de la Eternulo elhakas fajran flamon.
8 Liwu la Yehova limagwedeza chipululu; Yehova amagwedeza chipululu cha Kadesi.
La voĉo de la Eternulo skuas dezerton, La Eternulo skuas la dezerton Kadeŝ.
9 Liwu la Yehova limapindapinda mibawa ndi kuyeretsa nkhalango. Ndipo mʼNyumba mwake onse amafuwula kuti, “Ulemerero!”
La voĉo de la Eternulo igas cervinojn naski, kaj nudigas arbarojn; Kaj en Lia templo ĉio parolas pri Lia gloro.
10 Yehova amakhala pamwamba pa madzi osefukira, Yehova ndiye mfumu kwamuyaya.
La Eternulo regis en la tempo de la diluvo, La Eternulo restos Reĝo eterne.
11 Yehova amapereka mphamvu kwa anthu ake; Yehova amadalitsa anthu ake ndi mtendere.
La Eternulo donos forton al Sia popolo, La Eternulo benos Sian popolon per paco.