< Masalimo 29 >
1 Salimo la Davide. Perekani kwa Yehova, inu anthu amphamvu, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
A Psalm of David. Give to the LORD, O ye mighty, give to the LORD glory and strength.
2 Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake, pembedzani Yehova mwa kukongola kwa chiyero chake.
Give to the LORD, the glory due to his name; worship the LORD in the beauty of holiness.
3 Liwu la Yehova lili pamwamba pa madzi; Mulungu waulemerero abangula, Yehova abangula pamwamba pa madzi amphamvu.
The voice of the LORD [is] upon the waters: the God of glory thundereth: the LORD [is] upon many waters.
4 Liwu la Yehova ndi lamphamvu; liwu la Yehova ndi laulemerero.
The voice of the LORD [is] powerful; the voice of the LORD [is] full of majesty.
5 Liwu la Yehova limathyola mikungudza; Yehova amathyolathyola mikungudza ya ku Lebanoni.
The voice of the LORD breaketh the cedars; yes, the LORD breaketh the cedars of Lebanon.
6 Iye amachititsa Lebanoni kulumphalumpha ngati mwana wangʼombe, Siriyoni ngati mwana wa njati:
He maketh them also to skip like a calf; Lebanon and Sirion like a young unicorn.
7 Liwu la Yehova limakantha ngati kungʼanima kwa mphenzi.
The voice of the LORD divideth the flames of fire.
8 Liwu la Yehova limagwedeza chipululu; Yehova amagwedeza chipululu cha Kadesi.
The voice of the LORD shaketh the wilderness; the LORD shaketh the wilderness of Kadesh.
9 Liwu la Yehova limapindapinda mibawa ndi kuyeretsa nkhalango. Ndipo mʼNyumba mwake onse amafuwula kuti, “Ulemerero!”
The voice of the LORD maketh the hinds to calve, and maketh bare the forests: and in his temple doth every one speak of [his] glory.
10 Yehova amakhala pamwamba pa madzi osefukira, Yehova ndiye mfumu kwamuyaya.
The LORD sitteth upon the flood; yes, the LORD sitteth king for ever.
11 Yehova amapereka mphamvu kwa anthu ake; Yehova amadalitsa anthu ake ndi mtendere.
The LORD will give strength to his people; the LORD will bless his people with peace.