< Masalimo 29 >

1 Salimo la Davide. Perekani kwa Yehova, inu anthu amphamvu, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
Давидов псалом. Отдайте Господу, вие синове на силните, Отдайте Господу слава и могъщество.
2 Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake, pembedzani Yehova mwa kukongola kwa chiyero chake.
Отдайте Господу дължимата на името Му слава; Поклонете се Господу в света премяна.
3 Liwu la Yehova lili pamwamba pa madzi; Mulungu waulemerero abangula, Yehova abangula pamwamba pa madzi amphamvu.
Гласът Господен е над водите; Бог на славата гърми: Господ гърми над големите води,
4 Liwu la Yehova ndi lamphamvu; liwu la Yehova ndi laulemerero.
Гласът Господен е силен; Гласът Господен е величествен.
5 Liwu la Yehova limathyola mikungudza; Yehova amathyolathyola mikungudza ya ku Lebanoni.
Гласът Господен троши кедри; Да! Господ троши ливанските кедри,
6 Iye amachititsa Lebanoni kulumphalumpha ngati mwana wangʼombe, Siriyoni ngati mwana wa njati:
И прави да скачат като юнец, Ливан и Сирион като див вол в младостта си.
7 Liwu la Yehova limakantha ngati kungʼanima kwa mphenzi.
Гласът Господен разцепва огнените пламъци.
8 Liwu la Yehova limagwedeza chipululu; Yehova amagwedeza chipululu cha Kadesi.
Гласът Господен разтърсва пустинята; Господ разтърсва пустинята Кадис.
9 Liwu la Yehova limapindapinda mibawa ndi kuyeretsa nkhalango. Ndipo mʼNyumba mwake onse amafuwula kuti, “Ulemerero!”
Гласът Господен прави да раждат кошутите, И оголва лесовете; А в храма Му всеки възгласява Слава!
10 Yehova amakhala pamwamba pa madzi osefukira, Yehova ndiye mfumu kwamuyaya.
Господ седна Цар над Потопа; Да! Господ седна Цар до века.
11 Yehova amapereka mphamvu kwa anthu ake; Yehova amadalitsa anthu ake ndi mtendere.
Господ ще даде сила на людете Си; Господ ще благослови людете Си с мир.

< Masalimo 29 >