< Masalimo 28 >
1 Salimo la Davide. Kwa Inu ine ndiyitana, Yehova ndinu Thanthwe langa; musakhale osamva kwa ine. Pakuti mukapitirira kukhala chete, ndidzakhala ngati iwo amene atsikira ku dzenje.
Av David. Till dig, HERRE, ropar jag; min klippa, var icke stum mot mig. Ja, var icke tyst mot mig, så att jag bliver lik dem som fara ned i graven.
2 Imvani kupempha chifundo kwanga pomwe ndikuyitana kwa Inu kuti mundithandize, pomwe ndikukweza manja anga kuloza ku malo anu oyeretsetsa.
Hör mina böners ljud, när jag ropar till dig, när jag upplyfter mina händer mot det allraheligaste i din helgedom.
3 Musandikokere kutali pamodzi ndi anthu oyipa, pamodzi ndi iwo amene amachita zoyipa, amene amayankhula mwachikondi ndi anzawo koma akusunga chiwembu mʼmitima mwawo.
Tag mig icke bort med de ogudaktiga och med ogärningsmännen, som tala vänligt med sin nästa men hava ondska i sina hjärtan.
4 Muwabwezere chifukwa cha zochita zawo ndi ntchito zawo zoyipa; abwezereni chifuwa cha zimene manja awo achita ndipo mubweretse pa iwo zimene zowayenera.
Giv dem efter deras gärningar och efter deras onda väsende, giv dem efter deras händers verk, vedergäll dem vad de hava gjort.
5 Popeza iwowo sakhudzidwa ndi ntchito za Yehova, ndi zimene manja ake anazichita, Iye adzawakhadzula ndipo sadzawathandizanso.
Ty de akta icke på HERRENS gärningar, icke på hans händer verk; därför skall han slå dem ned och ej mer bygga upp dem.
6 Matamando apite kwa Yehova, popeza Iye wamva kupempha chifundo kwanga.
Lovad vare HERREN, ty han har hört mina böners ljud!
7 Yehova ndiye mphamvu yanga ndi chishango changa; mtima wanga umadalira Iye, ndipo Ine ndathandizidwa. Mtima wanga umalumphalumpha chifukwa cha chimwemwe ndipo ndidzayamika Iye mʼnyimbo.
HERREN är min starkhet och min sköld; på honom förtröstade mitt hjärta. Och jag vart hulpen, därför fröjdar sig mitt hjärta, och med min sång vill jag tacka honom.
8 Yehova ndi mphamvu ya anthu ake, linga la chipulumutso kwa wodzozedwa wake.
HERREN är sitt folks starkhet, och ett frälsningens värn är han för sin smorde.
9 Pulumutsani anthu anu ndipo mudalitse cholowa chanu; mukhale mʼbusa wawo ndipo muwakweze kwamuyaya.
Fräls ditt folk och välsigna din arvedel, och var deras herde och bär dem till evig tid.