< Masalimo 28 >

1 Salimo la Davide. Kwa Inu ine ndiyitana, Yehova ndinu Thanthwe langa; musakhale osamva kwa ine. Pakuti mukapitirira kukhala chete, ndidzakhala ngati iwo amene atsikira ku dzenje.
К Тебе, Господи, воззову, Боже мой: да не премолчиши от мене: да не когда премолчиши от мене, и уподоблюся низходящым в ров.
2 Imvani kupempha chifundo kwanga pomwe ndikuyitana kwa Inu kuti mundithandize, pomwe ndikukweza manja anga kuloza ku malo anu oyeretsetsa.
Услыши, Господи, глас моления моего, внегда молитимися к Тебе, внегда воздети ми руце мои ко храму святому Твоему.
3 Musandikokere kutali pamodzi ndi anthu oyipa, pamodzi ndi iwo amene amachita zoyipa, amene amayankhula mwachikondi ndi anzawo koma akusunga chiwembu mʼmitima mwawo.
Не привлецы мене со грешники, и с делающими неправду не погуби мене, глаголющими мир с ближними своими, злая же в сердцах своих.
4 Muwabwezere chifukwa cha zochita zawo ndi ntchito zawo zoyipa; abwezereni chifuwa cha zimene manja awo achita ndipo mubweretse pa iwo zimene zowayenera.
Даждь им, Господи, по делом их и по лукавству начинаний их, по делом руку их даждь им, воздаждь воздаяние их им.
5 Popeza iwowo sakhudzidwa ndi ntchito za Yehova, ndi zimene manja ake anazichita, Iye adzawakhadzula ndipo sadzawathandizanso.
Яко не разумеша в дела Господня и в дела руку Его: разориши я и не созиждеши я.
6 Matamando apite kwa Yehova, popeza Iye wamva kupempha chifundo kwanga.
Благословен Господь, яко услыша глас моления моего.
7 Yehova ndiye mphamvu yanga ndi chishango changa; mtima wanga umadalira Iye, ndipo Ine ndathandizidwa. Mtima wanga umalumphalumpha chifukwa cha chimwemwe ndipo ndidzayamika Iye mʼnyimbo.
Господь помощник мой и защититель мой: на Него упова сердце мое, и поможе ми, и процвете плоть моя: и волею моею исповемся Ему.
8 Yehova ndi mphamvu ya anthu ake, linga la chipulumutso kwa wodzozedwa wake.
Господь утверждение людий Своих и защититель спасений Христа Своего есть.
9 Pulumutsani anthu anu ndipo mudalitse cholowa chanu; mukhale mʼbusa wawo ndipo muwakweze kwamuyaya.
Спаси люди Твоя, и благослови достояние Твое, и упаси я, и возми я до века.

< Masalimo 28 >