< Masalimo 28 >
1 Salimo la Davide. Kwa Inu ine ndiyitana, Yehova ndinu Thanthwe langa; musakhale osamva kwa ine. Pakuti mukapitirira kukhala chete, ndidzakhala ngati iwo amene atsikira ku dzenje.
A ti clamarei, ó Senhor, Rocha minha; não emudeças para comigo: se te calares para comigo, fique eu semelhante aos que descem ao abismo.
2 Imvani kupempha chifundo kwanga pomwe ndikuyitana kwa Inu kuti mundithandize, pomwe ndikukweza manja anga kuloza ku malo anu oyeretsetsa.
Ouve a voz das minhas suplicas, quando a ti clamar, quando levantar as minhas mãos para o teu santo oráculo.
3 Musandikokere kutali pamodzi ndi anthu oyipa, pamodzi ndi iwo amene amachita zoyipa, amene amayankhula mwachikondi ndi anzawo koma akusunga chiwembu mʼmitima mwawo.
Não me arremesses com os ímpios e com os que obram a iniquidade; que falam de paz ao seu próximo, mas tem mal nos seus corações.
4 Muwabwezere chifukwa cha zochita zawo ndi ntchito zawo zoyipa; abwezereni chifuwa cha zimene manja awo achita ndipo mubweretse pa iwo zimene zowayenera.
Dá-lhes segundo as suas obras e segundo a malícia dos seus esforços; dá-lhes conforme a obra das suas mãos; torna-lhes a sua recompensa.
5 Popeza iwowo sakhudzidwa ndi ntchito za Yehova, ndi zimene manja ake anazichita, Iye adzawakhadzula ndipo sadzawathandizanso.
Porquanto não atendem às obras do Senhor, nem à obra das suas mãos; pelo que ele os derribará e não os reedificará.
6 Matamando apite kwa Yehova, popeza Iye wamva kupempha chifundo kwanga.
Bendito seja o Senhor, porque ouviu a voz das minhas suplicas.
7 Yehova ndiye mphamvu yanga ndi chishango changa; mtima wanga umadalira Iye, ndipo Ine ndathandizidwa. Mtima wanga umalumphalumpha chifukwa cha chimwemwe ndipo ndidzayamika Iye mʼnyimbo.
O Senhor é a minha força e o meu escudo; nele confiou o meu coração, e fui socorrido: pelo que o meu coração salta de prazer, e com o meu canto o louvarei.
8 Yehova ndi mphamvu ya anthu ake, linga la chipulumutso kwa wodzozedwa wake.
O Senhor é a força deles: também é a força salvadora do seu ungido.
9 Pulumutsani anthu anu ndipo mudalitse cholowa chanu; mukhale mʼbusa wawo ndipo muwakweze kwamuyaya.
Salva o teu povo, e abençoa a tua herança; e apascenta-os e exalta-os para sempre.