< Masalimo 28 >
1 Salimo la Davide. Kwa Inu ine ndiyitana, Yehova ndinu Thanthwe langa; musakhale osamva kwa ine. Pakuti mukapitirira kukhala chete, ndidzakhala ngati iwo amene atsikira ku dzenje.
Ihubo likaDavida. Ngikhala Kuwe, Oh Thixo, Dwala lami; ungangivaleli indlebe Yakho. Phela nxa ulokhu uthule ngizakuba njengalabo asebengene egodini.
2 Imvani kupempha chifundo kwanga pomwe ndikuyitana kwa Inu kuti mundithandize, pomwe ndikukweza manja anga kuloza ku malo anu oyeretsetsa.
Zwana ukukhala kwami ngicela umusa, nxa ngikhala Kuwe ngicela usizo, nxa ngiphakamisela izandla zami eNdaweni Yakho eNgcwelengcwele.
3 Musandikokere kutali pamodzi ndi anthu oyipa, pamodzi ndi iwo amene amachita zoyipa, amene amayankhula mwachikondi ndi anzawo koma akusunga chiwembu mʼmitima mwawo.
Ungangihuduli ndawonye lababi, lalabo abenza ububi, abakhuluma kamnandi labomakhelwane kodwa begcine ububi ezinhliziyweni zabo.
4 Muwabwezere chifukwa cha zochita zawo ndi ntchito zawo zoyipa; abwezereni chifuwa cha zimene manja awo achita ndipo mubweretse pa iwo zimene zowayenera.
Bajezisele izenzo zabo kanye lemisebenzi yabo emibi; bajezisele imisebenzi yezandla zabo, ubaphindisele ngokubafaneleyo.
5 Popeza iwowo sakhudzidwa ndi ntchito za Yehova, ndi zimene manja ake anazichita, Iye adzawakhadzula ndipo sadzawathandizanso.
Njengoba bengananzi imisebenzi kaThixo lalokho okwenziwe yizandla zakhe, uzababhidlizela phansi angaphindi ababumbe futhi.
6 Matamando apite kwa Yehova, popeza Iye wamva kupempha chifundo kwanga.
Udumo kalube kuye uThixo, ngoba ukuzwile ukukhala kwami ngicela umusa.
7 Yehova ndiye mphamvu yanga ndi chishango changa; mtima wanga umadalira Iye, ndipo Ine ndathandizidwa. Mtima wanga umalumphalumpha chifukwa cha chimwemwe ndipo ndidzayamika Iye mʼnyimbo.
UThixo ungamandla ami lesihlangu sami; inhliziyo yami yethemba Kuye, ngiyancedwa. Inhliziyo yami iyaqolotsha ngentokozo njalo ngizambonga ngehubo.
8 Yehova ndi mphamvu ya anthu ake, linga la chipulumutso kwa wodzozedwa wake.
UThixo ungamandla abantu bakhe, inqaba yensindiso yogcotshiweyo wakhe.
9 Pulumutsani anthu anu ndipo mudalitse cholowa chanu; mukhale mʼbusa wawo ndipo muwakweze kwamuyaya.
Sindisa abantu Bakho ubusise ilifa lakho; woba ngumelusi wabo ubathwale lanininini.