< Masalimo 28 >

1 Salimo la Davide. Kwa Inu ine ndiyitana, Yehova ndinu Thanthwe langa; musakhale osamva kwa ine. Pakuti mukapitirira kukhala chete, ndidzakhala ngati iwo amene atsikira ku dzenje.
[Psalm lal David] O LEUM GOD su langoeyu, nga pang nu sum. Lohng tung luk! Kom fin tia topukyu, Nga ac fah welulos su tufokla nu infulan misa.
2 Imvani kupempha chifundo kwanga pomwe ndikuyitana kwa Inu kuti mundithandize, pomwe ndikukweza manja anga kuloza ku malo anu oyeretsetsa.
Lohngyu ke nga pang in suk kasru sum, Ke nga asroeak pouk nu ke Tempul mutal sum.
3 Musandikokere kutali pamodzi ndi anthu oyipa, pamodzi ndi iwo amene amachita zoyipa, amene amayankhula mwachikondi ndi anzawo koma akusunga chiwembu mʼmitima mwawo.
Nikmet nununkeyu yurin mwet koluk, Yurin mwet su oru ma koluk — Mwet su kulang na likin pusraclos, A insialos sessesla ke srunga.
4 Muwabwezere chifukwa cha zochita zawo ndi ntchito zawo zoyipa; abwezereni chifuwa cha zimene manja awo achita ndipo mubweretse pa iwo zimene zowayenera.
Sang kai nu selos ke orekma koluk lalos, Ke ma koluk elos orala. Kaelos ke ma nukewa elos oru. Sang nu selos topken orekma koluk lalos!
5 Popeza iwowo sakhudzidwa ndi ntchito za Yehova, ndi zimene manja ake anazichita, Iye adzawakhadzula ndipo sadzawathandizanso.
Elos tiana lohang nu ke ma LEUM GOD El oru Ku nu ke orekma lun paol. Ke ma inge El ac fah kaelos Ac kunauselosla nwe tok.
6 Matamando apite kwa Yehova, popeza Iye wamva kupempha chifundo kwanga.
Kaksakin LEUM GOD, Tuh El lohng pusren kwafe luk.
7 Yehova ndiye mphamvu yanga ndi chishango changa; mtima wanga umadalira Iye, ndipo Ine ndathandizidwa. Mtima wanga umalumphalumpha chifukwa cha chimwemwe ndipo ndidzayamika Iye mʼnyimbo.
LEUM GOD El karinginyu ac kasreyu; Nga lulalfongi in El. El kasreyu ac akenganyeyu; Nga kaksakunul ke pusren on in engan.
8 Yehova ndi mphamvu ya anthu ake, linga la chipulumutso kwa wodzozedwa wake.
LEUM GOD El karingin mwet lal; El kasru ac molela tokosra su El sulela.
9 Pulumutsani anthu anu ndipo mudalitse cholowa chanu; mukhale mʼbusa wawo ndipo muwakweze kwamuyaya.
LEUM GOD, molela mwet lom, Ac akinsewowoyalos su ma lom. Kom in mwet shepherd lalos, Ac karinganulos nwe tok ma pahtpat.

< Masalimo 28 >