< Masalimo 28 >

1 Salimo la Davide. Kwa Inu ine ndiyitana, Yehova ndinu Thanthwe langa; musakhale osamva kwa ine. Pakuti mukapitirira kukhala chete, ndidzakhala ngati iwo amene atsikira ku dzenje.
To thee, O Jehovah, I will call. My rock, be not thou deaf to me, lest, if thou be silent to me, I become like those who go down into the pit.
2 Imvani kupempha chifundo kwanga pomwe ndikuyitana kwa Inu kuti mundithandize, pomwe ndikukweza manja anga kuloza ku malo anu oyeretsetsa.
Hear the voice of my supplications when I cry to thee, when I lift up my hands toward thy holy oracle.
3 Musandikokere kutali pamodzi ndi anthu oyipa, pamodzi ndi iwo amene amachita zoyipa, amene amayankhula mwachikondi ndi anzawo koma akusunga chiwembu mʼmitima mwawo.
Draw me not away with the wicked, and with the workers of iniquity, who speak peace with their neighbors, but mischief is in their hearts.
4 Muwabwezere chifukwa cha zochita zawo ndi ntchito zawo zoyipa; abwezereni chifuwa cha zimene manja awo achita ndipo mubweretse pa iwo zimene zowayenera.
Give them according to their work, and according to the wickedness of their doings. Give them after the operation of their hands. Render to them their recompense,
5 Popeza iwowo sakhudzidwa ndi ntchito za Yehova, ndi zimene manja ake anazichita, Iye adzawakhadzula ndipo sadzawathandizanso.
because they regard not the works of Jehovah, nor the operation of his hands. He will break them down and not build them up.
6 Matamando apite kwa Yehova, popeza Iye wamva kupempha chifundo kwanga.
Blessed be Jehovah, because he has heard the voice of my supplications.
7 Yehova ndiye mphamvu yanga ndi chishango changa; mtima wanga umadalira Iye, ndipo Ine ndathandizidwa. Mtima wanga umalumphalumpha chifukwa cha chimwemwe ndipo ndidzayamika Iye mʼnyimbo.
Jehovah is my strength and my shield. My heart has trusted in him, and I am helped. Therefore my heart greatly rejoices, and with my song I will praise him.
8 Yehova ndi mphamvu ya anthu ake, linga la chipulumutso kwa wodzozedwa wake.
Jehovah is their strength, and he is a stronghold of salvation to his anointed.
9 Pulumutsani anthu anu ndipo mudalitse cholowa chanu; mukhale mʼbusa wawo ndipo muwakweze kwamuyaya.
Save thy people, and bless thine inheritance. Be their shepherd also, and bear them up forever.

< Masalimo 28 >