< Masalimo 27 >

1 Salimo la Davide. Yehova ndiye kuwunika kwanga ndi chipulumutso changa; ndidzaopa yani? Yehova ndi linga la moyo wanga; ndidzachita mantha ndi yani?
Psalm Dawida. PAN jest moją światłością i moim zbawieniem, kogóż będę się bać? PAN jest mocą mego życia, kogóż mam się lękać?
2 Pamene anthu oyipa abwera kudzalimbana nane kudzadya mnofu wanga, pamene adani anga ndi achiwembu andithira nkhondo, iwo adzapunthwa ndi kugwa.
Gdy złoczyńcy, moi przeciwnicy i wrogowie, wystąpili przeciwko mnie, aby pożreć moje ciało, potknęli się i upadli.
3 Ngakhale gulu lankhondo lindizinge, mtima wanga sudzaopa. Ngakhale nkhondo itayambika kulimbana nane, ngakhale nthawi imeneyo, ine ndidzalimbika mtima.
Choćby wojsko rozbiło naprzeciw mnie obóz, moje serce się nie ulęknie; choćby wojna wybuchła przeciw mnie, nawet wtedy będę ufał.
4 Chinthu chimodzi chokha chimene ndipempha kwa Yehova, ichi ndi chimene ndidzachifunafuna: kuti ndikhale mʼNyumba ya Yehova masiku onse a moyo wanga, ndi kuyangʼana kukongola kwa Yehova, ndi kumufunafuna Iye mʼNyumba yake.
O jedno proszę PANA i o to będę zabiegał: abym mieszkał w domu PANA po wszystkie dni mego życia, abym oglądał piękno PANA i dowiadywał się w jego świątyni.
5 Pakuti pa tsiku la msautso Iye adzanditeteza mʼmalo ake okhalamo; adzandibisa mʼkati mwa Nyumba yake ndi kukhazika ine pamwamba pa thanthwe.
Skryje mnie bowiem w dniu niedoli w swoim przybytku, schowa mnie w ukryciu swego namiotu [i] wyniesie mnie na skałę.
6 Kotero mutu wanga udzakwezedwa kuposa adani anga amene andizungulira; pa Nyumba yake ndidzapereka nsembe ndi mfuwu wachimwemwe; ndidzayimba nyimbo kwa Yehova.
A teraz moja głowa będzie wzniesiona nad moimi nieprzyjaciółmi, którzy mnie otaczają; będę składał w jego przybytku ofiary radości, będę śpiewał i oddawał PANU chwałę.
7 Imvani mawu anga pamene ndiyitana Inu Yehova mundichitire chifundo ndipo mundiyankhe.
Usłysz, PANIE, mój głos, [gdy] wołam; zmiłuj się nade mną i wysłuchaj mnie.
8 Mtima wanga ukuti kwa Inu, “Funafuna nkhope yake!” Nkhope yanu Yehova ndidzayifunafuna.
[Gdy mówiłeś]: Szukajcie mojego oblicza, moje serce mówiło do ciebie: Twojego oblicza, PANIE, będę szukać.
9 Musandibisire nkhope yanu, musamubweze mtumiki wanu mwamkwiyo; mwakhala muli thandizo langa. Musandikane kapena kunditaya, Inu Mulungu Mpulumutsi wanga.
Nie ukrywaj przede mną twojego oblicza ani nie odtrącaj w gniewie swego sługi; ty jesteś moją pomocą, nie opuszczaj mnie i nie odchodź, Boże mego zbawienia.
10 Ngakhale abambo ndi amayi anga anditaya Yehova adzandisamala.
Choćby ojciec i matka opuścili mnie, to PAN mnie przygarnie.
11 Phunzitseni njira yanu Inu Yehova, munditsogolere mʼnjira yowongoka chifukwa cha ondizunza.
Naucz mnie, PANIE, twojej drogi i prowadź mnie ścieżką prostą ze względu na moich wrogów.
12 Musandipereke ku zokhumba za adani anga, pakuti mboni zambiri zauka kutsutsana nane ndipo zikundiopseza.
Nie wydawaj mnie na pastwę moich nieprzyjaciół, bo powstali przeciwko mnie fałszywi świadkowie i ci, którzy dyszą okrucieństwem.
13 Ine ndikutsimikiza mtima za zimenezi; ndidzaona ubwino wa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
[Zniechęciłbym się], gdybym nie wierzył, że będę oglądał dobroć PANA w ziemi żyjących.
14 Dikirani pa Yehova; khalani anyonga ndipo limbani mtima nimudikire Yehova.
Oczekuj PANA, bądź dzielny, [a on] umocni twoje serce; oczekuj więc PANA.

< Masalimo 27 >