< Masalimo 27 >

1 Salimo la Davide. Yehova ndiye kuwunika kwanga ndi chipulumutso changa; ndidzaopa yani? Yehova ndi linga la moyo wanga; ndidzachita mantha ndi yani?
Jehovah is my light and my salvation, whom shall I fear? Jehovah is the strength of my life, of whom shall I be afraid?
2 Pamene anthu oyipa abwera kudzalimbana nane kudzadya mnofu wanga, pamene adani anga ndi achiwembu andithira nkhondo, iwo adzapunthwa ndi kugwa.
When evildoers came upon me to eat up my flesh, even my adversaries and my foes, they stumbled and fell.
3 Ngakhale gulu lankhondo lindizinge, mtima wanga sudzaopa. Ngakhale nkhondo itayambika kulimbana nane, ngakhale nthawi imeneyo, ine ndidzalimbika mtima.
Though an army should encamp against me, my heart shall not fear. Though war should rise against me, even then I will be confident.
4 Chinthu chimodzi chokha chimene ndipempha kwa Yehova, ichi ndi chimene ndidzachifunafuna: kuti ndikhale mʼNyumba ya Yehova masiku onse a moyo wanga, ndi kuyangʼana kukongola kwa Yehova, ndi kumufunafuna Iye mʼNyumba yake.
One thing I have asked of Jehovah, that I will seek after, that I may dwell in the house of Jehovah all the days of my life, to behold the beauty of Jehovah, and to inquire in his temple.
5 Pakuti pa tsiku la msautso Iye adzanditeteza mʼmalo ake okhalamo; adzandibisa mʼkati mwa Nyumba yake ndi kukhazika ine pamwamba pa thanthwe.
For in the day of trouble he will hide me in his pavilion. In the covert of his tabernacle he will hide me. He will lift me up upon a rock.
6 Kotero mutu wanga udzakwezedwa kuposa adani anga amene andizungulira; pa Nyumba yake ndidzapereka nsembe ndi mfuwu wachimwemwe; ndidzayimba nyimbo kwa Yehova.
And now my head shall be lifted up above my enemies round about me. And I will offer in his tabernacle sacrifices of joy. I will sing, yea, I will sing praises to Jehovah.
7 Imvani mawu anga pamene ndiyitana Inu Yehova mundichitire chifundo ndipo mundiyankhe.
Hear, O Jehovah, when I cry with my voice. Have mercy also upon me, and answer me.
8 Mtima wanga ukuti kwa Inu, “Funafuna nkhope yake!” Nkhope yanu Yehova ndidzayifunafuna.
My heart said to thee, I have sought thy face. O Jehovah, I will seek thy face.
9 Musandibisire nkhope yanu, musamubweze mtumiki wanu mwamkwiyo; mwakhala muli thandizo langa. Musandikane kapena kunditaya, Inu Mulungu Mpulumutsi wanga.
Hide not thy face from me. Put not thy servant away in anger. Thou have been my help. Cast me not off, nor forsake me, O God of my salvation.
10 Ngakhale abambo ndi amayi anga anditaya Yehova adzandisamala.
When my father and my mother forsake me, then Jehovah will take me up.
11 Phunzitseni njira yanu Inu Yehova, munditsogolere mʼnjira yowongoka chifukwa cha ondizunza.
Teach me thy way, O Jehovah, and lead me in a plain path, because of my enemies.
12 Musandipereke ku zokhumba za adani anga, pakuti mboni zambiri zauka kutsutsana nane ndipo zikundiopseza.
Deliver me not over to the will of my adversaries. For false witnesses are risen up against me, and such as breathe out cruelty.
13 Ine ndikutsimikiza mtima za zimenezi; ndidzaona ubwino wa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
I believe that I shall see the goodness of Jehovah in the land of the living.
14 Dikirani pa Yehova; khalani anyonga ndipo limbani mtima nimudikire Yehova.
Wait for Jehovah. Be strong, and let thy heart take courage. Yea, wait thou for Jehovah.

< Masalimo 27 >