< Masalimo 27 >
1 Salimo la Davide. Yehova ndiye kuwunika kwanga ndi chipulumutso changa; ndidzaopa yani? Yehova ndi linga la moyo wanga; ndidzachita mantha ndi yani?
Bawipa taw ka maihchoei ingkaw ka hulnaak na awm hy - u nu kak kqih bai kaw? Bawipa taw ka hqingnaak vawngcak na awm hy - u nu kak kqih re bai kaw?
2 Pamene anthu oyipa abwera kudzalimbana nane kudzadya mnofu wanga, pamene adani anga ndi achiwembu andithira nkhondo, iwo adzapunthwa ndi kugwa.
Ka sa daih aham thlak chekhqi ing ni pan unawh ka qaalkhqi ingkaw ka thunkhakhqi ing amim tu awh ce bah kawm usaw tlu kawm uh.
3 Ngakhale gulu lankhondo lindizinge, mtima wanga sudzaopa. Ngakhale nkhondo itayambika kulimbana nane, ngakhale nthawi imeneyo, ine ndidzalimbika mtima.
Qalkap ing nik chung khoep seiawm, kak kawlung am thyn qoe tikaw; tangboek ing ni boeng qoe seiawm kak kawlung yp khak kaw.
4 Chinthu chimodzi chokha chimene ndipempha kwa Yehova, ichi ndi chimene ndidzachifunafuna: kuti ndikhale mʼNyumba ya Yehova masiku onse a moyo wanga, ndi kuyangʼana kukongola kwa Yehova, ndi kumufunafuna Iye mʼNyumba yake.
Bawipa venawh ik-oeih pynoet doeng thoeh nyng, ka thoeh taw veni; ka hqing khui pyt Bawipa im awh awm aham ingkaw Bawipa a myi daw soeih ce toek doena a bawkim khuiawh amah sui ve doeng ni.
5 Pakuti pa tsiku la msautso Iye adzanditeteza mʼmalo ake okhalamo; adzandibisa mʼkati mwa Nyumba yake ndi kukhazika ine pamwamba pa thanthwe.
Ikawtih kyinaak ka um awh ce a awmnaak hun awh kai ce ngaihding cana ni awm sak kaw; a hizan im awmnaak khuiawh ni thuh kawmsaw lungnu awh ce ak sang na nim hawih kaw.
6 Kotero mutu wanga udzakwezedwa kuposa adani anga amene andizungulira; pa Nyumba yake ndidzapereka nsembe ndi mfuwu wachimwemwe; ndidzayimba nyimbo kwa Yehova.
Cawhtaw kai anik chung khoep ka qaalkhqik khanawh ka luu ve zoeksang kaw; a hizan im awh zeel doena khy nawh lucik nawn nyng saw; Bawipa kyihcah ing laa sa hawh kawng nyng.
7 Imvani mawu anga pamene ndiyitana Inu Yehova mundichitire chifundo ndipo mundiyankhe.
Aw Bawipa, ka nik khy awh ce kak awi ngai law lah; nim qeen nawhtaw nim hlat lah.
8 Mtima wanga ukuti kwa Inu, “Funafuna nkhope yake!” Nkhope yanu Yehova ndidzayifunafuna.
Kak kawlung ing “A haai sui lah!” ni tina hy. Bawipa nang haai ni ka sui hly.
9 Musandibisire nkhope yanu, musamubweze mtumiki wanu mwamkwiyo; mwakhala muli thandizo langa. Musandikane kapena kunditaya, Inu Mulungu Mpulumutsi wanga.
Na haai ce koeh thuh valh nawh, na tyihzawih ve koeh mang taak; nang taw kai anik bawmkung ni. Aw Khawsa ka hulkung, koeh ni qoeng nawhtaw koeh ni cen taak.
10 Ngakhale abambo ndi amayi anga anditaya Yehova adzandisamala.
Ka pa ingkaw ka nu ing ni cehta seiawm, Bawipa ing ni do ngai kaw.
11 Phunzitseni njira yanu Inu Yehova, munditsogolere mʼnjira yowongoka chifukwa cha ondizunza.
Aw Bawipa, na lam ce ni cawng sak nawh; kai anik thekhanaakkhqi awh na lap dyng awh ni sawi lah.
12 Musandipereke ku zokhumba za adani anga, pakuti mboni zambiri zauka kutsutsana nane ndipo zikundiopseza.
Ka qaalkhqi ngaihnaak awh kai ce koeh ni pe, amak thym dyihthingkhqi ing ni thawh sih unawh, amak leek ben awi ce amik kqawn a dawngawh.
13 Ine ndikutsimikiza mtima za zimenezi; ndidzaona ubwino wa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
Ka hqingnaak qam awh ve Bawipa a leeknaak hu ngai kawng tinawh yp qu na mang kang nyng.
14 Dikirani pa Yehova; khalani anyonga ndipo limbani mtima nimudikire Yehova.
Bawipa mah qeh lah; kawlung cak doena nak tha awm sak nawh, Bawipa mah qeh lah.