< Masalimo 26 >

1 Salimo la Davide. Weruzeni Inu Yehova pakuti ndakhala moyo wosalakwa. Ndadalira Yehova popanda kugwedezeka.
Un Salmo de David. Confirma que soy inocente, Señor, porque he actuado con integridad, y he confiado en el Señor sin falta.
2 Patseni mayeso, Inu Yehova ndipo ndiyeseni, santhulani mtima wanga ndi maganizo anga;
Examíname, Señor, pruébame; investiga mi corazón y mi mente.
3 pakuti chikondi chanu chili pamaso panga nthawi zonse, ndipo ndimayenda mʼchoonadi chanu nthawi zonse.
Porque yo siempre recuerdo tu amor fiel, y sigo tu verdad.
4 Ine sindikhala pansi pamodzi ndi anthu achinyengo, kapena kufunsa nzeru kwa achiphamaso.
No me junto con mentirosos, ni me asocio con hipócritas.
5 Ndimanyansidwa ndi msonkhano wa anthu ochita zoyipa ndipo ndimakana kukhala pansi pamodzi ndi oyipa.
Me rehúso a estar junto a aquellos que hacen el mal, y no me veré envuelto con los malvados.
6 Ndimasamba mʼmanja mwanga kuonetsa kusalakwa kwanga ndi kupita kukatumikira pa guwa lanu la nsembe, Inu Yehova,
Lavo mis manos para mostrar mi inocencia. Vengo a adorar a tu altar, Señor,
7 kulengeza mofuwula za matamando anu ndi kuwuza onse za ntchito zanu zodabwitsa.
cantando mis agradecimientos, contando todas las cosas maravillosas cosas que has hecho.
8 Ndimakonda Nyumba imene Inu Yehova mumakhalamo, malo amene ulemerero wanu umapezekako.
Señor, amo tu casa, el lugar donde vives en tu gloria.
9 Musachotse moyo wanga pamodzi ndi ochimwa, moyo wanga pamodzi ndi anthu akupha anzawo,
Por favor, no me lances lejos con los pecadores. No me incluyas con aquellos que cometieron asesinatos,
10 amene mʼmanja mwawo muli ndondomeko zoyipa, dzanja lawo lamanja ladzaza ndi ziphuphu.
y cuyas manos cargan sus planes malvados y sobornos.
11 Koma ine ndimakhala moyo wosalakwa; mu msonkhano wa anthu anu ndidzatamanda Yehova.
Porque yo no hago eso, yo actúo con integridad. ¡Sálvame, y ten gracia conmigo!
12 Ndayima pa malo wopanda zovuta ndipo ndidzatamanda Yehova mu msonkhano waukulu.
Estoy a favor de lo que es correcto, y alabaré al Señor cuando nos reunamos a adorarle.

< Masalimo 26 >