< Masalimo 26 >
1 Salimo la Davide. Weruzeni Inu Yehova pakuti ndakhala moyo wosalakwa. Ndadalira Yehova popanda kugwedezeka.
Фэ-мь дрептате, Доамне, кэч умблу ын невиновэцие ши мэ ынкред ын Домнул фэрэ шовэире!
2 Patseni mayeso, Inu Yehova ndipo ndiyeseni, santhulani mtima wanga ndi maganizo anga;
Черчетязэ-мэ, Доамне, ынчаркэ-мэ, трече-мь прин купторул де фок рэрункий ши инима!
3 pakuti chikondi chanu chili pamaso panga nthawi zonse, ndipo ndimayenda mʼchoonadi chanu nthawi zonse.
Кэч бунэтатя Та есте ынаинтя окилор мей ши умблу ын адевэрул Тэу.
4 Ine sindikhala pansi pamodzi ndi anthu achinyengo, kapena kufunsa nzeru kwa achiphamaso.
Ну шед ымпреунэ ку оамений минчиношь ши ну мерг ымпреунэ ку оамений виклень.
5 Ndimanyansidwa ndi msonkhano wa anthu ochita zoyipa ndipo ndimakana kukhala pansi pamodzi ndi oyipa.
Урэск адунаря челор че фак рэул ши ну стау ымпреунэ ку чей рэй.
6 Ndimasamba mʼmanja mwanga kuonetsa kusalakwa kwanga ndi kupita kukatumikira pa guwa lanu la nsembe, Inu Yehova,
Ымь спэл мыниле ын невиновэцие ши аша ынконжор алтарул Тэу, Доамне,
7 kulengeza mofuwula za matamando anu ndi kuwuza onse za ntchito zanu zodabwitsa.
ка сэ избукнеск ын мулцумирь ши сэ историсеск тоате минуниле Тале.
8 Ndimakonda Nyumba imene Inu Yehova mumakhalamo, malo amene ulemerero wanu umapezekako.
Доамне, еу юбеск локашул Касей Тале ши локул ын каре локуеште слава Та.
9 Musachotse moyo wanga pamodzi ndi ochimwa, moyo wanga pamodzi ndi anthu akupha anzawo,
Ну-мь луа суфлетул ымпреунэ ку пэкэтоший, нич вяца ку оамений каре варсэ сынӂе,
10 amene mʼmanja mwawo muli ndondomeko zoyipa, dzanja lawo lamanja ladzaza ndi ziphuphu.
але кэрор мынь сунт нелеӂюите ши а кэрор дряптэ есте плинэ де митэ!
11 Koma ine ndimakhala moyo wosalakwa; mu msonkhano wa anthu anu ndidzatamanda Yehova.
Еу умблу ын неприхэнире; избэвеште-мэ ши ай милэ де мине!
12 Ndayima pa malo wopanda zovuta ndipo ndidzatamanda Yehova mu msonkhano waukulu.
Пичорул меу стэ пе каля чя дряптэ: вой бинекувынта пе Домнул ын адунэрь.