< Masalimo 26 >

1 Salimo la Davide. Weruzeni Inu Yehova pakuti ndakhala moyo wosalakwa. Ndadalira Yehova popanda kugwedezeka.
Av David. Søm meg til min rett, Herre! for eg hev fare fram i mi uskyld, og til Herren hev eg sett mi lit uruggeleg.
2 Patseni mayeso, Inu Yehova ndipo ndiyeseni, santhulani mtima wanga ndi maganizo anga;
Prøv meg, Herre, og freista meg, ransaka mine nyro og mitt hjarta!
3 pakuti chikondi chanu chili pamaso panga nthawi zonse, ndipo ndimayenda mʼchoonadi chanu nthawi zonse.
For din nåde er for mine augo, og eg ferdast i di sanning.
4 Ine sindikhala pansi pamodzi ndi anthu achinyengo, kapena kufunsa nzeru kwa achiphamaso.
Eg sit ikkje saman med falske menner og gjeng ikkje inn hjå fule folk.
5 Ndimanyansidwa ndi msonkhano wa anthu ochita zoyipa ndipo ndimakana kukhala pansi pamodzi ndi oyipa.
Eg hatar samkoma av illmenne, og hjå dei ugudlege sit eg ikkje.
6 Ndimasamba mʼmanja mwanga kuonetsa kusalakwa kwanga ndi kupita kukatumikira pa guwa lanu la nsembe, Inu Yehova,
Eg tvær mine hender i uskyld og vil gjerne ferdast um ditt altar, Herre,
7 kulengeza mofuwula za matamando anu ndi kuwuza onse za ntchito zanu zodabwitsa.
til å kveda lydt med lovsongs røyst og fortelja um alle dine under.
8 Ndimakonda Nyumba imene Inu Yehova mumakhalamo, malo amene ulemerero wanu umapezekako.
Herre, eg elskar di husvist og den stad der din herlegdom bur.
9 Musachotse moyo wanga pamodzi ndi ochimwa, moyo wanga pamodzi ndi anthu akupha anzawo,
Rykk ikkje mi sjæl burt med syndarar eller mitt liv med blodgiruge menner,
10 amene mʼmanja mwawo muli ndondomeko zoyipa, dzanja lawo lamanja ladzaza ndi ziphuphu.
som hev skamgjerd i sine hender og si høgre hand full av mutor.
11 Koma ine ndimakhala moyo wosalakwa; mu msonkhano wa anthu anu ndidzatamanda Yehova.
Men eg fer fram i mi uskyld; løys meg ut og ver meg nådig!
12 Ndayima pa malo wopanda zovuta ndipo ndidzatamanda Yehova mu msonkhano waukulu.
Min fot stend på slettlende. I samlingarne skal eg lova Herren.

< Masalimo 26 >