< Masalimo 26 >
1 Salimo la Davide. Weruzeni Inu Yehova pakuti ndakhala moyo wosalakwa. Ndadalira Yehova popanda kugwedezeka.
In finem, Psalmus David. Iudica me Domine, quoniam ego in innocentia mea ingressus sum: et in Domino sperans non infirmabor.
2 Patseni mayeso, Inu Yehova ndipo ndiyeseni, santhulani mtima wanga ndi maganizo anga;
Proba me Domine, et tenta me: ure renes meos et cor meum.
3 pakuti chikondi chanu chili pamaso panga nthawi zonse, ndipo ndimayenda mʼchoonadi chanu nthawi zonse.
Quoniam misericordia tua ante oculos meos est: et complacui in veritate tua.
4 Ine sindikhala pansi pamodzi ndi anthu achinyengo, kapena kufunsa nzeru kwa achiphamaso.
Non sedi cum concilio vanitatis: et cum iniqua gerentibus non introibo.
5 Ndimanyansidwa ndi msonkhano wa anthu ochita zoyipa ndipo ndimakana kukhala pansi pamodzi ndi oyipa.
Odivi ecclesiam malignantium: et cum impiis non sedebo.
6 Ndimasamba mʼmanja mwanga kuonetsa kusalakwa kwanga ndi kupita kukatumikira pa guwa lanu la nsembe, Inu Yehova,
Lavabo inter innocentes manus meas: et circumdabo altare tuum Domine:
7 kulengeza mofuwula za matamando anu ndi kuwuza onse za ntchito zanu zodabwitsa.
Ut audiam vocem laudis, et enarrem universa mirabilia tua.
8 Ndimakonda Nyumba imene Inu Yehova mumakhalamo, malo amene ulemerero wanu umapezekako.
Domine dilexi decorem domus tuæ, et locum habitationis gloriæ tuæ.
9 Musachotse moyo wanga pamodzi ndi ochimwa, moyo wanga pamodzi ndi anthu akupha anzawo,
Ne perdas cum impiis Deus animam meam, et cum viris sanguinum vitam meam:
10 amene mʼmanja mwawo muli ndondomeko zoyipa, dzanja lawo lamanja ladzaza ndi ziphuphu.
In quorum manibus iniquitates sunt: dextera eorum repleta est muneribus.
11 Koma ine ndimakhala moyo wosalakwa; mu msonkhano wa anthu anu ndidzatamanda Yehova.
Ego autem in innocentia mea ingressus sum: redime me, et miserere mei.
12 Ndayima pa malo wopanda zovuta ndipo ndidzatamanda Yehova mu msonkhano waukulu.
Pes meus stetit in directo: in ecclesiis benedicam te Domine.