< Masalimo 26 >

1 Salimo la Davide. Weruzeni Inu Yehova pakuti ndakhala moyo wosalakwa. Ndadalira Yehova popanda kugwedezeka.
Daavidin virsi. Auta minut oikeuteeni, Herra, sillä minä olen vaeltanut nuhteettomasti ja turvaan horjumatta Herraan.
2 Patseni mayeso, Inu Yehova ndipo ndiyeseni, santhulani mtima wanga ndi maganizo anga;
Tutki minua, Herra, ja pane minut koetukselle, koettele minun munaskuuni ja sydämeni.
3 pakuti chikondi chanu chili pamaso panga nthawi zonse, ndipo ndimayenda mʼchoonadi chanu nthawi zonse.
Sillä sinun armosi on minun silmäini edessä, ja minä olen vaeltanut sinun totuudessasi.
4 Ine sindikhala pansi pamodzi ndi anthu achinyengo, kapena kufunsa nzeru kwa achiphamaso.
En minä istu valheen miesten seurassa enkä kulje salakavalain kanssa.
5 Ndimanyansidwa ndi msonkhano wa anthu ochita zoyipa ndipo ndimakana kukhala pansi pamodzi ndi oyipa.
Minä vihaan pahojen seuraa enkä istu jumalattomien parissa.
6 Ndimasamba mʼmanja mwanga kuonetsa kusalakwa kwanga ndi kupita kukatumikira pa guwa lanu la nsembe, Inu Yehova,
Minä pesen käteni viattomuudessa, ja astun kulkueessa sinun alttarisi ympäri, Herra,
7 kulengeza mofuwula za matamando anu ndi kuwuza onse za ntchito zanu zodabwitsa.
antaakseni kuulua kiitokseni äänen ja julistaakseni kaikkia sinun ihmeitäsi.
8 Ndimakonda Nyumba imene Inu Yehova mumakhalamo, malo amene ulemerero wanu umapezekako.
Herra, minä rakastan sinun huonettasi, sinun asuinsijaasi, sitä paikkaa, jossa sinun kirkkautesi asuu.
9 Musachotse moyo wanga pamodzi ndi ochimwa, moyo wanga pamodzi ndi anthu akupha anzawo,
Älä tempaa pois minun sieluani syntisten kanssa äläkä minun henkeäni verenvuodattajain kanssa,
10 amene mʼmanja mwawo muli ndondomeko zoyipa, dzanja lawo lamanja ladzaza ndi ziphuphu.
joiden käsiä ilkityö tahraa, joiden oikea käsi on lahjuksia täynnä.
11 Koma ine ndimakhala moyo wosalakwa; mu msonkhano wa anthu anu ndidzatamanda Yehova.
Mutta minä vaellan nuhteettomasti; vapahda minut ja ole minulle armollinen.
12 Ndayima pa malo wopanda zovuta ndipo ndidzatamanda Yehova mu msonkhano waukulu.
Minun jalkani seisoo tasaisella maalla; seurakunnan kokouksissa minä kiitän Herraa.

< Masalimo 26 >