< Masalimo 25 >
1 Salimo la Davide. Kwa Inu Yehova, ndipereka moyo wanga.
Псалом Давидів. До Тебе, Господи, я підношу мою душу.
2 Ndimadalira Inu Mulungu wanga. Musalole kuti ndichite manyazi kapena kuti adani anga andipambane.
Боже мій, на Тебе надію покладаю; тож не дай мені вкритися соромом, нехай вороги не радіють перемозі наді мною.
3 Aliyense amene amayembekezera kwa Ambuye sadzachititsidwa manyazi koma achinyengo ndiwo adzachititsidwe manyazi ndipo sadzakhala ndi chodzitetezera.
Не дай жодному з тих, хто на Тебе надію покладає, бути посоромленим, але нехай вкриються ганьбою ті, хто безпідставно чинить віроломство.
4 Ndidziwitseni njira zanu Inu Yehova, phunzitseni mayendedwe anu;
Покажи мені, шляхи Твої, Господи, навчи мене стежок Твоїх.
5 tsogolereni mʼchoonadi chanu ndi kundiphunzitsa, pakuti Inu ndinu Mulungu mpulumutsi wanga, ndipo chiyembekezo changa chili mwa Inu tsiku lonse.
Веди мене істиною Твоєю й навчи мене, адже Ти – Бог спасіння мого, на Тебе я надію покладаю щодня.
6 Kumbukirani Inu Yehova chifundo ndi chikondi chanu chachikulu, pakuti ndi zakalekale.
Згадай, Господи, любов Твою й Твоє милосердя, адже вони споконвіку.
7 Musakumbukire machimo a ubwana wanga ndi makhalidwe anga owukira; molingana ndi chikondi chanu ndikumbukireni ine, pakuti Inu Yehova ndinu wabwino.
Гріхів юності моєї й беззаконь моїх не згадуй, [але] заради милосердя Твого згадай мене, заради доброти Твоєї, Господи.
8 Yehova ndi wabwino ndi wolungama; choncho Iye akulangiza ochimwa mʼnjira yake.
Добрий і справедливий Господь, тому наставляє грішників на [істинний] шлях.
9 Amatsogolera odzichepetsa kuti achite zolungama ndipo amawaphunzitsa njira zake.
Він спрямовує смиренних до справедливості й покірливих навчає дороги Своєї.
10 Njira zonse za Yehova ndi zachikondi ndi zokhulupirika kwa iwo amene amasunga zofuna za pangano lake.
Усі стежки Господні – милість та істина для тих, хто дотримується Його Завіту й одкровень.
11 Chifukwa cha dzina lanu, Inu Yehova, khululukireni mphulupulu zanga, ngakhale kuti ndi zochuluka.
Заради імені Твого, Господи, прости беззаконня моє, бо велике воно.
12 Tsono ndani munthu amene amaopa Yehova? Yehova adzamulangiza njira yoti ayitsate.
Хто той муж, що Господа боїться? Вкаже йому [Бог] дорогу, яку треба обрати.
13 Iye adzakhala pa ulemerero masiku ake onse, ndipo zidzukulu zake zidzalandira dziko ngati cholowa chawo.
Душа його житиме в достатку, і нащадки його успадкують землю.
14 Yehova amawulula chinsinsi chake kwa iwo amene amamuopa; amawulula pangano lake kwa iwowo.
Таємницю [Свою]Господь[довіряє] тим, хто боїться Його, і Завіт Свій відкриває їм.
15 Maso anga ali pa Yehova nthawi zonse, pakuti ndi Iye yekha amene adzawonjola mapazi anga mu msampha.
Очі мої завжди [звернені] до Господа, бо Він звільняє ноги мої із пастки.
16 Tembenukirani kwa ine ndipo mundikomere mtima, pakuti ndili ndekhandekha ndipo ndikuzunzika.
Зглянься на мене й змилуйся наді мною, бо я самотній і пригнічений.
17 Masautso a mu mtima mwanga achulukirachulukira; masuleni ku zowawa zanga.
Скорботи мого серця примножилися – виведи мене зі страждань моїх.
18 Penyani mazunzo anga ndi zovuta zanga ndipo mufafanize machimo anga onse.
Поглянь на приниження моє й муку мою і прости усі гріхи мої.
19 Onani mmene adani anga achulukira ndi momwe chidani chawo ndi ine chakulira.
Подивися на ворогів моїх, які численні вони стали і якою ненавистю лютою ненавидять мене.
20 Tetezani moyo wanga ndi kundilanditsa; musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndimathawira kwa Inu.
Збережи мою душу й визволи мене, не дай мені вкритися ганьбою, адже на Тебе надію покладаю.
21 Kukhulupirika ndi kulungama kwanga kunditeteze, chifukwa chiyembekezo changa chili mwa Inu.
Невинність і справедливість нехай стережуть мене, бо на Тебе я покладаю надію.
22 Wombolani Israeli Inu Mulungu, ku mavuto ake onse!
Визволи, Боже, Ізраїля від усіх скорбот його!