< Masalimo 25 >

1 Salimo la Davide. Kwa Inu Yehova, ndipereka moyo wanga.
Av David. Till dig, HERRE, upplyfter jag min själ.
2 Ndimadalira Inu Mulungu wanga. Musalole kuti ndichite manyazi kapena kuti adani anga andipambane.
Min Gud, på dig förtröstar jag; låt mig icke komma på skam, låt icke mina fiender fröjda sig över mig.
3 Aliyense amene amayembekezera kwa Ambuye sadzachititsidwa manyazi koma achinyengo ndiwo adzachititsidwe manyazi ndipo sadzakhala ndi chodzitetezera.
Nej, ingen kommer på skam, som förbidar dig; på skam kommer de som, utan sak, handla trolöst.
4 Ndidziwitseni njira zanu Inu Yehova, phunzitseni mayendedwe anu;
HERRE, kungör mig dina vägar, lär mig dina stigar.
5 tsogolereni mʼchoonadi chanu ndi kundiphunzitsa, pakuti Inu ndinu Mulungu mpulumutsi wanga, ndipo chiyembekezo changa chili mwa Inu tsiku lonse.
Led mig i din sanning, och lär mig, ty du är min frälsnings Gud; dig förbidar jag alltid.
6 Kumbukirani Inu Yehova chifundo ndi chikondi chanu chachikulu, pakuti ndi zakalekale.
Tänk, HERRE, på din barmhärtighet och din nåd, ty de äro av evighet.
7 Musakumbukire machimo a ubwana wanga ndi makhalidwe anga owukira; molingana ndi chikondi chanu ndikumbukireni ine, pakuti Inu Yehova ndinu wabwino.
Tänk icke på min ungdoms synder och på mina överträdelser, utan tänk på mig efter din nåd, för din godhets skull, HERRE.
8 Yehova ndi wabwino ndi wolungama; choncho Iye akulangiza ochimwa mʼnjira yake.
HERREN är god och rättfärdig, därför undervisar han syndare om vägen.
9 Amatsogolera odzichepetsa kuti achite zolungama ndipo amawaphunzitsa njira zake.
Han leder de ödmjuka rätt, han lär de ödmjuka sin väg.
10 Njira zonse za Yehova ndi zachikondi ndi zokhulupirika kwa iwo amene amasunga zofuna za pangano lake.
Alla HERRENS vägar äro nåd och trofasthet för dem som hålla hans förbund och vittnesbörd.
11 Chifukwa cha dzina lanu, Inu Yehova, khululukireni mphulupulu zanga, ngakhale kuti ndi zochuluka.
För ditt namns skull, HERRE, förlåt min missgärning, ty den är stor.
12 Tsono ndani munthu amene amaopa Yehova? Yehova adzamulangiza njira yoti ayitsate.
Finnes det en man som fruktar HERREN, då undervisar han honom om den väg han bör välja.
13 Iye adzakhala pa ulemerero masiku ake onse, ndipo zidzukulu zake zidzalandira dziko ngati cholowa chawo.
Han själv skall leva i lycka, och hans efterkommande skola besitta landet.
14 Yehova amawulula chinsinsi chake kwa iwo amene amamuopa; amawulula pangano lake kwa iwowo.
HERREN har sin umgängelse med dem som frukta honom, och sitt förbund vill han kungöra för dem.
15 Maso anga ali pa Yehova nthawi zonse, pakuti ndi Iye yekha amene adzawonjola mapazi anga mu msampha.
Mina ögon se alltid till HERREN, ty han drager mina fötter ur nätet.
16 Tembenukirani kwa ine ndipo mundikomere mtima, pakuti ndili ndekhandekha ndipo ndikuzunzika.
Vänd dig till mig och var mig nådig; ty jag är ensam och betryckt.
17 Masautso a mu mtima mwanga achulukirachulukira; masuleni ku zowawa zanga.
Mitt hjärtas ångest är stor; för mig ut ur mitt trångmål.
18 Penyani mazunzo anga ndi zovuta zanga ndipo mufafanize machimo anga onse.
Se till mitt lidande och min vedermöda, och förlåt mig alla mina synder.
19 Onani mmene adani anga achulukira ndi momwe chidani chawo ndi ine chakulira.
Se därtill att mina fiender äro så många och hata mig med orätt.
20 Tetezani moyo wanga ndi kundilanditsa; musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndimathawira kwa Inu.
Bevara min själ och rädda mig; låt mig icke komma på skam, ty jag tager min tillflykt till dig.
21 Kukhulupirika ndi kulungama kwanga kunditeteze, chifukwa chiyembekezo changa chili mwa Inu.
Ostrafflighet och redlighet bevare mig, ty jag förbidar dig.
22 Wombolani Israeli Inu Mulungu, ku mavuto ake onse!
Förlossa Israel, o Gud, ur all dess nöd. Alfabetisk psalm; se Poesi i Ordförkl.

< Masalimo 25 >