< Masalimo 25 >

1 Salimo la Davide. Kwa Inu Yehova, ndipereka moyo wanga.
A ti, oh SEÑOR, mi alma enaltece.
2 Ndimadalira Inu Mulungu wanga. Musalole kuti ndichite manyazi kapena kuti adani anga andipambane.
Oh Dios mío, he puesto mi fe en ti, no me avergüences; no permitas que mis enemigos se glorien sobre mí.
3 Aliyense amene amayembekezera kwa Ambuye sadzachititsidwa manyazi koma achinyengo ndiwo adzachititsidwe manyazi ndipo sadzakhala ndi chodzitetezera.
No se avergüence ningún siervo tuyo que en ti confía; serán avergonzados aquellos que se rebelan sin causa.
4 Ndidziwitseni njira zanu Inu Yehova, phunzitseni mayendedwe anu;
Muéstrame tus caminos, oh Señor; enséñame tus senderos.
5 tsogolereni mʼchoonadi chanu ndi kundiphunzitsa, pakuti Inu ndinu Mulungu mpulumutsi wanga, ndipo chiyembekezo changa chili mwa Inu tsiku lonse.
Sé mi guía y maestro de la manera verdadera; porque tú eres el Dios de mi salvación; Estoy esperando tu palabra todo el día.
6 Kumbukirani Inu Yehova chifundo ndi chikondi chanu chachikulu, pakuti ndi zakalekale.
Oh Señor, ten en cuenta tu compasión y tus misericordias; que son perpetuas.
7 Musakumbukire machimo a ubwana wanga ndi makhalidwe anga owukira; molingana ndi chikondi chanu ndikumbukireni ine, pakuti Inu Yehova ndinu wabwino.
No tengas en cuenta mis pecados cuando era joven, o mi maldad: deja que tu recuerdo de mí esté lleno de misericordia, oh Señor, por tu gran amor y bondad.
8 Yehova ndi wabwino ndi wolungama; choncho Iye akulangiza ochimwa mʼnjira yake.
Bueno y justo es el Señor: entonces él enseñará a los pecadores el camino.
9 Amatsogolera odzichepetsa kuti achite zolungama ndipo amawaphunzitsa njira zake.
Y guía para los pobres en espíritu: enseñará a los mansos el camino.
10 Njira zonse za Yehova ndi zachikondi ndi zokhulupirika kwa iwo amene amasunga zofuna za pangano lake.
Todos los caminos del Señor son misericordia y verdad para aquellos que mantienen su pacto y su testimonio.
11 Chifukwa cha dzina lanu, Inu Yehova, khululukireni mphulupulu zanga, ngakhale kuti ndi zochuluka.
Por tu nombre, oh Señor, permíteme tener perdón por mi pecado, que es muy grande.
12 Tsono ndani munthu amene amaopa Yehova? Yehova adzamulangiza njira yoti ayitsate.
Si un hombre tiene temor del Señor, el Señor le enseñará el camino que debe seguir,
13 Iye adzakhala pa ulemerero masiku ake onse, ndipo zidzukulu zake zidzalandira dziko ngati cholowa chawo.
gozará de bienestar, y su simiente tendrá la tierra por su herencia.
14 Yehova amawulula chinsinsi chake kwa iwo amene amamuopa; amawulula pangano lake kwa iwowo.
La comunión íntima de Jehová es con los que le temen, con aquellos en cuyo corazón está el temor de él; y a ellos hará conocer su pacto.
15 Maso anga ali pa Yehova nthawi zonse, pakuti ndi Iye yekha amene adzawonjola mapazi anga mu msampha.
Mis ojos se vuelven al Señor todo el tiempo; porque él sacará mis pies de la red.
16 Tembenukirani kwa ine ndipo mundikomere mtima, pakuti ndili ndekhandekha ndipo ndikuzunzika.
Mírame Señor ten misericordia de mí; porque estoy solo y preocupado.
17 Masautso a mu mtima mwanga achulukirachulukira; masuleni ku zowawa zanga.
Los problemas de mi corazón aumentan: Oh sácame de mis dolores.
18 Penyani mazunzo anga ndi zovuta zanga ndipo mufafanize machimo anga onse.
Mira mi penas y mi dolor; y perdona todos mis pecados.
19 Onani mmene adani anga achulukira ndi momwe chidani chawo ndi ine chakulira.
Mira cómo aumentan los que están en mi contra, con su odio violento me aborrecen.
20 Tetezani moyo wanga ndi kundilanditsa; musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndimathawira kwa Inu.
Guarda mi alma, y ​​arráncame fuera de peligro; no me avergüences, porque he puesto mi fe en ti.
21 Kukhulupirika ndi kulungama kwanga kunditeteze, chifukwa chiyembekezo changa chili mwa Inu.
Que mis caminos limpios y rectos me protejan, porque mi esperanza está en ti.
22 Wombolani Israeli Inu Mulungu, ku mavuto ake onse!
Dale a Israel salvación, oh Dios, de todas sus angustias.

< Masalimo 25 >