< Masalimo 25 >
1 Salimo la Davide. Kwa Inu Yehova, ndipereka moyo wanga.
К Теби, Господе, подижем душу своју.
2 Ndimadalira Inu Mulungu wanga. Musalole kuti ndichite manyazi kapena kuti adani anga andipambane.
Боже мој! У Тебе се уздам; не дај да се осрамотим, да ми се не свете непријатељи моји.
3 Aliyense amene amayembekezera kwa Ambuye sadzachititsidwa manyazi koma achinyengo ndiwo adzachititsidwe manyazi ndipo sadzakhala ndi chodzitetezera.
И који се год у Те уздају, неће се осрамотити; осрамотиће се они који се одмећу од Тебе беспутно.
4 Ndidziwitseni njira zanu Inu Yehova, phunzitseni mayendedwe anu;
Покажи ми, Господе, путеве своје, научи ме ходити стазама Твојим.
5 tsogolereni mʼchoonadi chanu ndi kundiphunzitsa, pakuti Inu ndinu Mulungu mpulumutsi wanga, ndipo chiyembekezo changa chili mwa Inu tsiku lonse.
Упути ме истини својој, и научи ме; јер си Ти Бог спасења мог, Теби се надам сваки дан.
6 Kumbukirani Inu Yehova chifundo ndi chikondi chanu chachikulu, pakuti ndi zakalekale.
Опомени се милосрђа свог, Господе, и милости своје; јер су откако је века.
7 Musakumbukire machimo a ubwana wanga ndi makhalidwe anga owukira; molingana ndi chikondi chanu ndikumbukireni ine, pakuti Inu Yehova ndinu wabwino.
Грехова младости моје, и мојих преступа не помињи; по милости својој помени мене, ради доброте своје, Господе!
8 Yehova ndi wabwino ndi wolungama; choncho Iye akulangiza ochimwa mʼnjira yake.
Добар је и праведан Господ; тога ради показује грешницима пут.
9 Amatsogolera odzichepetsa kuti achite zolungama ndipo amawaphunzitsa njira zake.
Упућује кротке истини, учи кротке ходити путем Његовим.
10 Njira zonse za Yehova ndi zachikondi ndi zokhulupirika kwa iwo amene amasunga zofuna za pangano lake.
Сви су путеви Господњи милост и истина онима који држе завет Његов и откривење Његово.
11 Chifukwa cha dzina lanu, Inu Yehova, khululukireni mphulupulu zanga, ngakhale kuti ndi zochuluka.
Ради имена свог, Господе, опрости грех мој, јер је велик.
12 Tsono ndani munthu amene amaopa Yehova? Yehova adzamulangiza njira yoti ayitsate.
Који се човек боји Господа? Он ће му показати који пут да изабере.
13 Iye adzakhala pa ulemerero masiku ake onse, ndipo zidzukulu zake zidzalandira dziko ngati cholowa chawo.
Душа ће његова у добру почивати, и семе ће његово владати земљом.
14 Yehova amawulula chinsinsi chake kwa iwo amene amamuopa; amawulula pangano lake kwa iwowo.
Тајна је Господња у оних који Га се боје, и завет свој јавља им.
15 Maso anga ali pa Yehova nthawi zonse, pakuti ndi Iye yekha amene adzawonjola mapazi anga mu msampha.
Очи су ми свагда управљене ка Господу, јер Он извлачи из замке ноге моје.
16 Tembenukirani kwa ine ndipo mundikomere mtima, pakuti ndili ndekhandekha ndipo ndikuzunzika.
Погледај ме и смилуј се на ме, јер сам инокосан и невољник.
17 Masautso a mu mtima mwanga achulukirachulukira; masuleni ku zowawa zanga.
Нек се рашири стиснуто срце моје, из тескобе моје извади ме.
18 Penyani mazunzo anga ndi zovuta zanga ndipo mufafanize machimo anga onse.
Види јаде моје и муку моју, и опрости ми све грехове моје.
19 Onani mmene adani anga achulukira ndi momwe chidani chawo ndi ine chakulira.
Погледај непријатеље моје како их је много и каквом ме пакосном ненавишћу ненавиде.
20 Tetezani moyo wanga ndi kundilanditsa; musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndimathawira kwa Inu.
Сачувај душу моју и избави ме; не дај да се осрамотим, јер се у Тебе уздам.
21 Kukhulupirika ndi kulungama kwanga kunditeteze, chifukwa chiyembekezo changa chili mwa Inu.
Безазленост и правда нека ме сачува, јер се у Тебе уздам.
22 Wombolani Israeli Inu Mulungu, ku mavuto ake onse!
Избави, Боже, Израиља од свих невоља његових.