< Masalimo 25 >

1 Salimo la Davide. Kwa Inu Yehova, ndipereka moyo wanga.
Psalmus David, in finem. Ad te Domine levavi animam meam:
2 Ndimadalira Inu Mulungu wanga. Musalole kuti ndichite manyazi kapena kuti adani anga andipambane.
Deus meus in te confido, non erubescam:
3 Aliyense amene amayembekezera kwa Ambuye sadzachititsidwa manyazi koma achinyengo ndiwo adzachititsidwe manyazi ndipo sadzakhala ndi chodzitetezera.
Neque irrideant me inimici mei: etenim universi, qui sustinent te, non confundentur.
4 Ndidziwitseni njira zanu Inu Yehova, phunzitseni mayendedwe anu;
Confundantur omnes iniqua agentes supervacue. Vias tuas Domine demonstra mihi: et semitas tuas edoce me.
5 tsogolereni mʼchoonadi chanu ndi kundiphunzitsa, pakuti Inu ndinu Mulungu mpulumutsi wanga, ndipo chiyembekezo changa chili mwa Inu tsiku lonse.
Dirige me in veritate tua, et doce me: quia tu es Deus salvator meus, et te sustinui tota die.
6 Kumbukirani Inu Yehova chifundo ndi chikondi chanu chachikulu, pakuti ndi zakalekale.
Reminiscere miserationum tuarum Domine, et misericordiarum tuarum, quae a saeculo sunt.
7 Musakumbukire machimo a ubwana wanga ndi makhalidwe anga owukira; molingana ndi chikondi chanu ndikumbukireni ine, pakuti Inu Yehova ndinu wabwino.
Delicta iuventutis meae, et ignorantias meas ne memineris. Secundum misericordiam tuam memento mei tu: propter bonitatem tuam Domine.
8 Yehova ndi wabwino ndi wolungama; choncho Iye akulangiza ochimwa mʼnjira yake.
Dulcis et rectus Dominus: propter hoc legem dabit delinquentibus in via.
9 Amatsogolera odzichepetsa kuti achite zolungama ndipo amawaphunzitsa njira zake.
Diriget mansuetos in iudicio: docebit mites vias suas.
10 Njira zonse za Yehova ndi zachikondi ndi zokhulupirika kwa iwo amene amasunga zofuna za pangano lake.
Universae viae Domini, misericordia et veritas, requirentibus testamentum eius et testimonia eius.
11 Chifukwa cha dzina lanu, Inu Yehova, khululukireni mphulupulu zanga, ngakhale kuti ndi zochuluka.
Propter nomen tuum Domine propitiaberis peccato meo: multum est enim.
12 Tsono ndani munthu amene amaopa Yehova? Yehova adzamulangiza njira yoti ayitsate.
Quis est homo qui timet Dominum? legem statuit ei in via, quam elegit.
13 Iye adzakhala pa ulemerero masiku ake onse, ndipo zidzukulu zake zidzalandira dziko ngati cholowa chawo.
Anima eius in bonis demorabitur: et semen eius hereditabit terram.
14 Yehova amawulula chinsinsi chake kwa iwo amene amamuopa; amawulula pangano lake kwa iwowo.
Firmamentum est Dominus timentibus eum: et testamentum ipsius ut manifestetur illis.
15 Maso anga ali pa Yehova nthawi zonse, pakuti ndi Iye yekha amene adzawonjola mapazi anga mu msampha.
Oculi mei semper ad Dominum: quoniam ipse evellet de laqueo pedes meos.
16 Tembenukirani kwa ine ndipo mundikomere mtima, pakuti ndili ndekhandekha ndipo ndikuzunzika.
Respice in me, et miserere mei: quia unicus et pauper sum ego.
17 Masautso a mu mtima mwanga achulukirachulukira; masuleni ku zowawa zanga.
Tribulationes cordis mei multiplicatae sunt: de necessitatibus meis erue me.
18 Penyani mazunzo anga ndi zovuta zanga ndipo mufafanize machimo anga onse.
Vide humilitatem meam, et laborem meum: et dimitte universa delicta mea.
19 Onani mmene adani anga achulukira ndi momwe chidani chawo ndi ine chakulira.
Respice inimicos meos quoniam multiplicati sunt, et odio iniquo oderunt me.
20 Tetezani moyo wanga ndi kundilanditsa; musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndimathawira kwa Inu.
Custodi animam meam, et erue me: non erubescam, quoniam speravi in te.
21 Kukhulupirika ndi kulungama kwanga kunditeteze, chifukwa chiyembekezo changa chili mwa Inu.
Innocentes et recti adhaeserunt mihi: quia sustinui te.
22 Wombolani Israeli Inu Mulungu, ku mavuto ake onse!
Libera Deus Israel ex omnibus tribulationibus suis.

< Masalimo 25 >