< Masalimo 25 >

1 Salimo la Davide. Kwa Inu Yehova, ndipereka moyo wanga.
ああヱホバよ わがたましひは汝をあふぎ望む
2 Ndimadalira Inu Mulungu wanga. Musalole kuti ndichite manyazi kapena kuti adani anga andipambane.
わが神よわれなんぢに依賴めり ねがはくはわれに愧をおはしめたまふなかれ わが仇のわれに勝誇ることなからしめたまへ
3 Aliyense amene amayembekezera kwa Ambuye sadzachititsidwa manyazi koma achinyengo ndiwo adzachititsidwe manyazi ndipo sadzakhala ndi chodzitetezera.
實になんぢを俟望むものははぢしめられず 故なくして信をうしなふものは愧をうけん
4 Ndidziwitseni njira zanu Inu Yehova, phunzitseni mayendedwe anu;
ヱホバよなんぢの大路をわれにしめし なんぢの徑をわれにをしへたまへ
5 tsogolereni mʼchoonadi chanu ndi kundiphunzitsa, pakuti Inu ndinu Mulungu mpulumutsi wanga, ndipo chiyembekezo changa chili mwa Inu tsiku lonse.
我をなんぢの眞理にみちびき我ををしへたまへ 汝はわがすくひの神なり われ終日なんぢを俟望む
6 Kumbukirani Inu Yehova chifundo ndi chikondi chanu chachikulu, pakuti ndi zakalekale.
なんぢのあはれみと仁慈とはいにしへより絶ずあり ヱホバよこれを思ひいだしたまへ
7 Musakumbukire machimo a ubwana wanga ndi makhalidwe anga owukira; molingana ndi chikondi chanu ndikumbukireni ine, pakuti Inu Yehova ndinu wabwino.
わがわかきときの罪とわが愆とはおもひいでたまふなかれ ヱホバよ汝のめぐみの故になんぢの仁慈にしたがひて我をおもひいでたまへ
8 Yehova ndi wabwino ndi wolungama; choncho Iye akulangiza ochimwa mʼnjira yake.
ヱホバはめぐみ深くして直くましませり 斯るがゆゑに道をつみびとにをしへ
9 Amatsogolera odzichepetsa kuti achite zolungama ndipo amawaphunzitsa njira zake.
謙だるものを正義にみちびきたまはん その道をへりくだる者にしめしたまはん
10 Njira zonse za Yehova ndi zachikondi ndi zokhulupirika kwa iwo amene amasunga zofuna za pangano lake.
ヱホバのもろもろの道はそのけいやくと證詞とをまもるものには仁慈なり眞理なり
11 Chifukwa cha dzina lanu, Inu Yehova, khululukireni mphulupulu zanga, ngakhale kuti ndi zochuluka.
わが不義はおほいなり ヱホバよ名のために之をゆるしたまへ
12 Tsono ndani munthu amene amaopa Yehova? Yehova adzamulangiza njira yoti ayitsate.
ヱホバをおそるる者はたれなるか 之にそのえらぶべき道をしめしたまはん
13 Iye adzakhala pa ulemerero masiku ake onse, ndipo zidzukulu zake zidzalandira dziko ngati cholowa chawo.
かかる人のたましひは平安にすまひ その裔はくにをつぐべし
14 Yehova amawulula chinsinsi chake kwa iwo amene amamuopa; amawulula pangano lake kwa iwowo.
ヱホバの親愛はヱホバをおそるる者とともにあり ヱホバはその契約をかれらに示したまはん
15 Maso anga ali pa Yehova nthawi zonse, pakuti ndi Iye yekha amene adzawonjola mapazi anga mu msampha.
わが目はつねにヱホバにむかふ ヱホバわがあしを網よりとりいだしたまふ可ればなり
16 Tembenukirani kwa ine ndipo mundikomere mtima, pakuti ndili ndekhandekha ndipo ndikuzunzika.
ねがはくは歸りきたりて我をあはれみたまへ われ獨わびしくまた苦しみをるなり
17 Masautso a mu mtima mwanga achulukirachulukira; masuleni ku zowawa zanga.
願くはわが心のうれへをゆるめ我をわざはひより脱かれしめたまへ
18 Penyani mazunzo anga ndi zovuta zanga ndipo mufafanize machimo anga onse.
わが患難わが辛苦をかへりみ わがすべての罪をゆるしたまへ
19 Onani mmene adani anga achulukira ndi momwe chidani chawo ndi ine chakulira.
わが仇をみたまへ かれらの數はおほし情なき憾をもてわれをにくめり
20 Tetezani moyo wanga ndi kundilanditsa; musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndimathawira kwa Inu.
わがたましひをまもり我をたすけたまへ われに愧をおはしめたまふなかれ 我なんぢに依賴めばなり
21 Kukhulupirika ndi kulungama kwanga kunditeteze, chifukwa chiyembekezo changa chili mwa Inu.
われなんぢを挨望むねがはくは完全と正直とわれをまもれかし
22 Wombolani Israeli Inu Mulungu, ku mavuto ake onse!
神よすべての憂よりイスラエルを贖ひいだしたまへ

< Masalimo 25 >