< Masalimo 25 >
1 Salimo la Davide. Kwa Inu Yehova, ndipereka moyo wanga.
Yon sòm David A Ou menm, O SENYÈ, mwen leve nanm mwen.
2 Ndimadalira Inu Mulungu wanga. Musalole kuti ndichite manyazi kapena kuti adani anga andipambane.
O Bondye mwen, nan Ou, mwen mete konfyans mwen. Pa kite mwen vin wont; pa kite lènmi m yo fè fèt sou mwen.
3 Aliyense amene amayembekezera kwa Ambuye sadzachititsidwa manyazi koma achinyengo ndiwo adzachititsidwe manyazi ndipo sadzakhala ndi chodzitetezera.
Anverite, nanpwen nan (sila) ki tann Ou yo ki va wont; (sila) ki fè konplo kont Ou san koz yo, va wont.
4 Ndidziwitseni njira zanu Inu Yehova, phunzitseni mayendedwe anu;
Fè m konnen pa Ou yo, O SENYÈ; enstwi m nan chemen Ou yo.
5 tsogolereni mʼchoonadi chanu ndi kundiphunzitsa, pakuti Inu ndinu Mulungu mpulumutsi wanga, ndipo chiyembekezo changa chili mwa Inu tsiku lonse.
Mennen mwen nan verite Ou e enstwi mwen, Paske se Ou menm ki Bondye delivrans mwen; se Ou m ap tann tout lajounen.
6 Kumbukirani Inu Yehova chifundo ndi chikondi chanu chachikulu, pakuti ndi zakalekale.
Sonje, O SENYÈ, mizerikòd Ou ak lanmou dous Ou a, Paske se yo ki la depi tan ale nèt.
7 Musakumbukire machimo a ubwana wanga ndi makhalidwe anga owukira; molingana ndi chikondi chanu ndikumbukireni ine, pakuti Inu Yehova ndinu wabwino.
Pa sonje peche jenès mwen yo, ni transgresyon mwen yo. Selon lanmou dous Ou, sonje mwen, Pou koz a bonte Ou, O SENYÈ.
8 Yehova ndi wabwino ndi wolungama; choncho Iye akulangiza ochimwa mʼnjira yake.
Bon e plen ladwati, se SENYÈ a; pou sa, Li enstwi pechè yo nan chemen an.
9 Amatsogolera odzichepetsa kuti achite zolungama ndipo amawaphunzitsa njira zake.
Li dirije enb yo nan jistis, e Li va enstwi enb yo nan chemen Li.
10 Njira zonse za Yehova ndi zachikondi ndi zokhulupirika kwa iwo amene amasunga zofuna za pangano lake.
Tout chemen Bondye se nan lanmou dous avèk verite pou (sila) ki kenbe akò Li yo ak temwayaj Li yo.
11 Chifukwa cha dzina lanu, Inu Yehova, khululukireni mphulupulu zanga, ngakhale kuti ndi zochuluka.
Pou koz a non Ou, O SENYÈ, padone inikite mwen, paske li anpil.
12 Tsono ndani munthu amene amaopa Yehova? Yehova adzamulangiza njira yoti ayitsate.
Kilès nonm nan ki gen krent SENYÈ a? Li va enstwi li nan chemen li ta dwe chwazi a.
13 Iye adzakhala pa ulemerero masiku ake onse, ndipo zidzukulu zake zidzalandira dziko ngati cholowa chawo.
Nanm li va viv alèz. Desandan li yo va resevwa eritaj peyi a.
14 Yehova amawulula chinsinsi chake kwa iwo amene amamuopa; amawulula pangano lake kwa iwowo.
Lamitye SENYÈ a se pou (sila) ki gen lakrent Li yo. Li va fè yo konnen akò Li.
15 Maso anga ali pa Yehova nthawi zonse, pakuti ndi Iye yekha amene adzawonjola mapazi anga mu msampha.
Zye m toujou vè SENYÈ a, paske Li va retire pye mwen nan pèlen an.
16 Tembenukirani kwa ine ndipo mundikomere mtima, pakuti ndili ndekhandekha ndipo ndikuzunzika.
Vire vè mwen e fè m gras, paske mwen abandone e aflije.
17 Masautso a mu mtima mwanga achulukirachulukira; masuleni ku zowawa zanga.
Twoub a kè m yo vin plis. Mennen m sòti nan gwo detrès sa a.
18 Penyani mazunzo anga ndi zovuta zanga ndipo mufafanize machimo anga onse.
Gade sou afliksyon mwen avèk twoub mwen yo, e padone tout peche mwen yo.
19 Onani mmene adani anga achulukira ndi momwe chidani chawo ndi ine chakulira.
Gade sou tout lènmi mwen yo, paske yo anpil. Epi yo rayi mwen avèk yon rayisman ki vyolan.
20 Tetezani moyo wanga ndi kundilanditsa; musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndimathawira kwa Inu.
Gade nanm mwen e delivre mwen. Pa kite m vin wont, paske mwen pran refij nan Ou menm.
21 Kukhulupirika ndi kulungama kwanga kunditeteze, chifukwa chiyembekezo changa chili mwa Inu.
Kite entegrite avèk ladwati pwoteje mwen, paske se Ou m ap tann.
22 Wombolani Israeli Inu Mulungu, ku mavuto ake onse!
Delivre Israël, O Bondye, sou tout twoub li yo.