< Masalimo 25 >
1 Salimo la Davide. Kwa Inu Yehova, ndipereka moyo wanga.
De David. O Éternel, j'élève mon âme à toi.
2 Ndimadalira Inu Mulungu wanga. Musalole kuti ndichite manyazi kapena kuti adani anga andipambane.
Mon Dieu, je mets en toi ma confiance: Que je ne sois pas couvert de confusion! Que mes ennemis ne se réjouissent pas à mon sujet!
3 Aliyense amene amayembekezera kwa Ambuye sadzachititsidwa manyazi koma achinyengo ndiwo adzachititsidwe manyazi ndipo sadzakhala ndi chodzitetezera.
Non, aucun de ceux qui s'attendent à toi Ne sera couvert de honte; Mais ils rougiront tous de honte, Ceux qui se révoltent injustement contre toi.
4 Ndidziwitseni njira zanu Inu Yehova, phunzitseni mayendedwe anu;
Éternel, fais-moi connaître tes voies; Enseigne-moi tes sentiers!
5 tsogolereni mʼchoonadi chanu ndi kundiphunzitsa, pakuti Inu ndinu Mulungu mpulumutsi wanga, ndipo chiyembekezo changa chili mwa Inu tsiku lonse.
Fais-moi marcher dans la voie de ta vérité, et instruis-moi; Car tu es le Dieu de mon salut: Je m'attends à toi chaque jour.
6 Kumbukirani Inu Yehova chifundo ndi chikondi chanu chachikulu, pakuti ndi zakalekale.
Éternel, souviens-toi de tes compassions et de tes bontés; Car elles sont de tout temps.
7 Musakumbukire machimo a ubwana wanga ndi makhalidwe anga owukira; molingana ndi chikondi chanu ndikumbukireni ine, pakuti Inu Yehova ndinu wabwino.
Ne te souviens pas des fautes de ma jeunesse, ni de mes péchés; Souviens-toi de moi, dans ta bonté, A cause de ta bienveillance, ô Éternel!
8 Yehova ndi wabwino ndi wolungama; choncho Iye akulangiza ochimwa mʼnjira yake.
L'Éternel est bon et droit; C'est pourquoi il montrera le chemin aux pécheurs.
9 Amatsogolera odzichepetsa kuti achite zolungama ndipo amawaphunzitsa njira zake.
Il fera marcher les humbles dans la justice; Il enseignera sa voie aux humbles.
10 Njira zonse za Yehova ndi zachikondi ndi zokhulupirika kwa iwo amene amasunga zofuna za pangano lake.
Tous les sentiers de l'Éternel ne sont que bonté et fidélité, Pour ceux qui gardent son alliance et ses commandements.
11 Chifukwa cha dzina lanu, Inu Yehova, khululukireni mphulupulu zanga, ngakhale kuti ndi zochuluka.
Pour l'amour de ton nom, ô Éternel, Tu pardonneras mon iniquité, bien qu'elle soît grande!
12 Tsono ndani munthu amene amaopa Yehova? Yehova adzamulangiza njira yoti ayitsate.
Quel est l'homme qui craint l'Éternel? L'Éternel lui enseignera le chemin qu'il doit choisir.
13 Iye adzakhala pa ulemerero masiku ake onse, ndipo zidzukulu zake zidzalandira dziko ngati cholowa chawo.
Son âme reposera au sein du bonheur. Et sa postérité possédera la terre.
14 Yehova amawulula chinsinsi chake kwa iwo amene amamuopa; amawulula pangano lake kwa iwowo.
Le secret de l'Éternel est pour ceux qui le craignent. Et il leur fait connaître son alliance.
15 Maso anga ali pa Yehova nthawi zonse, pakuti ndi Iye yekha amene adzawonjola mapazi anga mu msampha.
Mes yeux regardent sans cesse vers l'Éternel; Car il dégagera mes pieds du filet.
16 Tembenukirani kwa ine ndipo mundikomere mtima, pakuti ndili ndekhandekha ndipo ndikuzunzika.
Tourne-toi vers moi, prends pitié de moi; Car je suis seul et misérable!
17 Masautso a mu mtima mwanga achulukirachulukira; masuleni ku zowawa zanga.
La détresse de mon coeur augmente: Délivre-moi de mes angoisses!
18 Penyani mazunzo anga ndi zovuta zanga ndipo mufafanize machimo anga onse.
Vois ma misère et mon tourment. Et pardonne tous mes péchés!
19 Onani mmene adani anga achulukira ndi momwe chidani chawo ndi ine chakulira.
Vois combien mes ennemis sont nombreux Et de quelle violente haine ils sont animés contre moi.
20 Tetezani moyo wanga ndi kundilanditsa; musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndimathawira kwa Inu.
Garde mon âme et délivre-moi! Que je ne sois pas couvert de honte; Car j'ai cherché un refuge auprès de toi!
21 Kukhulupirika ndi kulungama kwanga kunditeteze, chifukwa chiyembekezo changa chili mwa Inu.
Que l'intégrité et la droiture me protègent; Car j'ai mis mon espoir en toi!
22 Wombolani Israeli Inu Mulungu, ku mavuto ake onse!
Dieu, délivre Israël De toutes ses détresses!