< Masalimo 25 >

1 Salimo la Davide. Kwa Inu Yehova, ndipereka moyo wanga.
Psaume de David. [Aleph.] Eternel, j'élève mon âme à toi.
2 Ndimadalira Inu Mulungu wanga. Musalole kuti ndichite manyazi kapena kuti adani anga andipambane.
[Beth.] Mon Dieu, je m'assure en toi, fais que je ne sois point confus, [et] que mes ennemis ne triomphent point de moi.
3 Aliyense amene amayembekezera kwa Ambuye sadzachititsidwa manyazi koma achinyengo ndiwo adzachititsidwe manyazi ndipo sadzakhala ndi chodzitetezera.
[Guimel.] Certes, pas un de ceux qui se confient en toi, ne sera confus; ceux qui agissent perfidement sans sujet seront confus.
4 Ndidziwitseni njira zanu Inu Yehova, phunzitseni mayendedwe anu;
[Daleth.] Eternel! fais-moi connaître tes voies, enseigne-moi tes sentiers.
5 tsogolereni mʼchoonadi chanu ndi kundiphunzitsa, pakuti Inu ndinu Mulungu mpulumutsi wanga, ndipo chiyembekezo changa chili mwa Inu tsiku lonse.
[He. Vau.] Fais-moi marcher selon la vérité, et m'enseigne; car tu es le Dieu de ma délivrance; je m'attends à toi tout le jour.
6 Kumbukirani Inu Yehova chifundo ndi chikondi chanu chachikulu, pakuti ndi zakalekale.
[Zain.] Eternel, souviens-toi de tes compassions et de tes gratuités; car elles sont de tout temps.
7 Musakumbukire machimo a ubwana wanga ndi makhalidwe anga owukira; molingana ndi chikondi chanu ndikumbukireni ine, pakuti Inu Yehova ndinu wabwino.
[Heth.] Ne te souviens point des péchés de ma jeunesse, ni de mes transgressions; selon ta gratuité souviens-toi de moi, pour l'amour de ta bonté, ô Eternel!
8 Yehova ndi wabwino ndi wolungama; choncho Iye akulangiza ochimwa mʼnjira yake.
[Teth.] L’Eternel est bon et droit, c'est pourquoi il enseignera aux pécheurs le chemin qu'ils doivent tenir.
9 Amatsogolera odzichepetsa kuti achite zolungama ndipo amawaphunzitsa njira zake.
[Jod.] Il fera marcher dans la justice les débonnaires, et il leur enseignera sa voie.
10 Njira zonse za Yehova ndi zachikondi ndi zokhulupirika kwa iwo amene amasunga zofuna za pangano lake.
[Caph.] Tous les sentiers de l'Eternel [sont] gratuité et vérité à ceux qui gardent son alliance et ses témoignages.
11 Chifukwa cha dzina lanu, Inu Yehova, khululukireni mphulupulu zanga, ngakhale kuti ndi zochuluka.
[Lamed.] Pour l'amour de ton Nom, ô Eternel! tu me pardonneras mon iniquité, quoiqu'elle soit grande.
12 Tsono ndani munthu amene amaopa Yehova? Yehova adzamulangiza njira yoti ayitsate.
[Mem.] Qui est l'homme qui craint l'Eternel? [L'Eternel] lui enseignera le chemin qu'il doit choisir.
13 Iye adzakhala pa ulemerero masiku ake onse, ndipo zidzukulu zake zidzalandira dziko ngati cholowa chawo.
[Nun.] Son âme logera au milieu des biens, et sa postérité possédera la terre en héritage.
14 Yehova amawulula chinsinsi chake kwa iwo amene amamuopa; amawulula pangano lake kwa iwowo.
[Samech.] Le secret de l'Eternel est pour ceux qui le craignent, et son alliance pour la leur donner à connaître.
15 Maso anga ali pa Yehova nthawi zonse, pakuti ndi Iye yekha amene adzawonjola mapazi anga mu msampha.
[Hajin.] Mes yeux sont continuellement sur l'Eternel; car c'est lui qui tirera mes pieds du filet.
16 Tembenukirani kwa ine ndipo mundikomere mtima, pakuti ndili ndekhandekha ndipo ndikuzunzika.
[Pe.] Tourne ta face vers moi, et aie pitié de moi; car je suis seul, et affligé.
17 Masautso a mu mtima mwanga achulukirachulukira; masuleni ku zowawa zanga.
[Tsade.] Les détresses de mon cœur se sont augmentées; tire-moi hors de mes angoisses.
18 Penyani mazunzo anga ndi zovuta zanga ndipo mufafanize machimo anga onse.
[Res.] Regarde mon affliction et mon travail, et me pardonne tous mes péchés.
19 Onani mmene adani anga achulukira ndi momwe chidani chawo ndi ine chakulira.
[Res.] Regarde mes ennemis, car ils sont en grand nombre, et ils me haïssent d'une haine [pleine] de violence.
20 Tetezani moyo wanga ndi kundilanditsa; musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndimathawira kwa Inu.
[Scin.] Garde mon âme, et me délivre; [fais] que je ne sois point confus; car je me suis retiré vers toi.
21 Kukhulupirika ndi kulungama kwanga kunditeteze, chifukwa chiyembekezo changa chili mwa Inu.
[Thau.] Que l'intégrité et la droiture me gardent; car je me suis attendu à toi.
22 Wombolani Israeli Inu Mulungu, ku mavuto ake onse!
[Pe.] Ô Dieu! rachète Israël de toutes ses détresses.

< Masalimo 25 >