< Masalimo 25 >

1 Salimo la Davide. Kwa Inu Yehova, ndipereka moyo wanga.
Davidin Psalmi. Sinun tykös, Herra, ylennän minä sieluni.
2 Ndimadalira Inu Mulungu wanga. Musalole kuti ndichite manyazi kapena kuti adani anga andipambane.
Minun Jumalani! sinuun minä turvaan, älä salli minua häväistä, ettei minun viholliseni iloitsisi minusta.
3 Aliyense amene amayembekezera kwa Ambuye sadzachititsidwa manyazi koma achinyengo ndiwo adzachititsidwe manyazi ndipo sadzakhala ndi chodzitetezera.
Sillä ei yksikään tule häpiään, joka sinua odottaa; mutta irralliset pilkkaajat saavat häpiän.
4 Ndidziwitseni njira zanu Inu Yehova, phunzitseni mayendedwe anu;
Herra, osoita minulle sinun ties, ja opeta minulle sinun polkus.
5 tsogolereni mʼchoonadi chanu ndi kundiphunzitsa, pakuti Inu ndinu Mulungu mpulumutsi wanga, ndipo chiyembekezo changa chili mwa Inu tsiku lonse.
Johdata minua totuudessas, ja opeta minua; sillä sinä olet Jumala, joka minua autat, yli päivää minä odotan sinua.
6 Kumbukirani Inu Yehova chifundo ndi chikondi chanu chachikulu, pakuti ndi zakalekale.
Muista, Herra, laupiuttas ja hyvyyttäs, joka maailman alusta on ollut.
7 Musakumbukire machimo a ubwana wanga ndi makhalidwe anga owukira; molingana ndi chikondi chanu ndikumbukireni ine, pakuti Inu Yehova ndinu wabwino.
Älä muista nuoruuteni syntejä ja ylitsekäymistäni; mutta muista minua sinun laupiutes jälkeen, sinun hyvyytes tähden, Herra!
8 Yehova ndi wabwino ndi wolungama; choncho Iye akulangiza ochimwa mʼnjira yake.
Herra on hyvä ja vakaa, sentähden saattaa hän syntiset tielle.
9 Amatsogolera odzichepetsa kuti achite zolungama ndipo amawaphunzitsa njira zake.
Hän johdattaa oikeudella raadollisen, ja opettaa siveille hänen tiensä.
10 Njira zonse za Yehova ndi zachikondi ndi zokhulupirika kwa iwo amene amasunga zofuna za pangano lake.
Kaikki Herran tiet ovat hyvyys ja totuus niille, jotka hänen liittonsa ja todistuksensa pitävät.
11 Chifukwa cha dzina lanu, Inu Yehova, khululukireni mphulupulu zanga, ngakhale kuti ndi zochuluka.
Sinun nimes tähden, Herra, ole armollinen minun pahalle teolleni, joka suuri on.
12 Tsono ndani munthu amene amaopa Yehova? Yehova adzamulangiza njira yoti ayitsate.
Kuka on se mies, joka Herraa pelkää? sillä hän opettaa parhaan tien.
13 Iye adzakhala pa ulemerero masiku ake onse, ndipo zidzukulu zake zidzalandira dziko ngati cholowa chawo.
Hänen sielunsa asuu hyvyydessä, ja hänen sikiänsä omistaa maan.
14 Yehova amawulula chinsinsi chake kwa iwo amene amamuopa; amawulula pangano lake kwa iwowo.
Herran salaisuus on niillä, jotka häntä pelkäävät, ja liittonsa ilmoittaa hän heille.
15 Maso anga ali pa Yehova nthawi zonse, pakuti ndi Iye yekha amene adzawonjola mapazi anga mu msampha.
Minun silmäni katsovat alati Herraa, sillä hän kirvoittaa minun jalkani verkosta.
16 Tembenukirani kwa ine ndipo mundikomere mtima, pakuti ndili ndekhandekha ndipo ndikuzunzika.
Käännä sinuas minun puoleeni, ja ole minulle armollinen; sillä minä olen yksinäinen ja raadollinen.
17 Masautso a mu mtima mwanga achulukirachulukira; masuleni ku zowawa zanga.
Minun sydämeni murheet ovat moninaiset: vie siis minua ulos tuskistani.
18 Penyani mazunzo anga ndi zovuta zanga ndipo mufafanize machimo anga onse.
Katsos minun vaivaisuuteni ja raadollisuuteni puoleen, ja anna kaikki minun syntini anteeksi.
19 Onani mmene adani anga achulukira ndi momwe chidani chawo ndi ine chakulira.
Katsos, kuinka monta vihollista minulla on? ja sulasta kateudesta he minua vihaavat.
20 Tetezani moyo wanga ndi kundilanditsa; musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndimathawira kwa Inu.
Varjele minun sieluni ja vapahda minua, älä laske minua häpiään; sillä sinuun minä turvaan.
21 Kukhulupirika ndi kulungama kwanga kunditeteze, chifukwa chiyembekezo changa chili mwa Inu.
Vakuus ja oikeus varjelkoon minua; sillä minä odotan sinua.
22 Wombolani Israeli Inu Mulungu, ku mavuto ake onse!
Jumala, vapahda Israel kaikista tuskistansa.

< Masalimo 25 >