< Masalimo 25 >

1 Salimo la Davide. Kwa Inu Yehova, ndipereka moyo wanga.
[A Psalm] of David. Unto thee, O LORD, do I lift up my soul.
2 Ndimadalira Inu Mulungu wanga. Musalole kuti ndichite manyazi kapena kuti adani anga andipambane.
O my God, in thee have I trusted, let me not be ashamed; let not mine enemies triumph over me.
3 Aliyense amene amayembekezera kwa Ambuye sadzachititsidwa manyazi koma achinyengo ndiwo adzachititsidwe manyazi ndipo sadzakhala ndi chodzitetezera.
Yea, none that wait on thee shall be ashamed: they shall be ashamed that deal treacherously without cause.
4 Ndidziwitseni njira zanu Inu Yehova, phunzitseni mayendedwe anu;
Shew me thy ways, O LORD; teach me thy paths.
5 tsogolereni mʼchoonadi chanu ndi kundiphunzitsa, pakuti Inu ndinu Mulungu mpulumutsi wanga, ndipo chiyembekezo changa chili mwa Inu tsiku lonse.
Guide me in thy truth, and teach me; for thou art the God of my salvation; on thee do I wait all the day.
6 Kumbukirani Inu Yehova chifundo ndi chikondi chanu chachikulu, pakuti ndi zakalekale.
Remember, O LORD, thy tender mercies and thy lovingkindnesses; for they have been ever of old.
7 Musakumbukire machimo a ubwana wanga ndi makhalidwe anga owukira; molingana ndi chikondi chanu ndikumbukireni ine, pakuti Inu Yehova ndinu wabwino.
Remember not the sins of my youth, nor my transgressions: according to thy lovingkindness remember thou me, for thy goodness’ sake, O LORD.
8 Yehova ndi wabwino ndi wolungama; choncho Iye akulangiza ochimwa mʼnjira yake.
Good and upright is the LORD: therefore will he instruct sinners in the way.
9 Amatsogolera odzichepetsa kuti achite zolungama ndipo amawaphunzitsa njira zake.
The meek will he guide in judgment: and the meek will he teach his way.
10 Njira zonse za Yehova ndi zachikondi ndi zokhulupirika kwa iwo amene amasunga zofuna za pangano lake.
All the paths of the LORD are lovingkindness and truth unto such as keep his covenant and his testimonies.
11 Chifukwa cha dzina lanu, Inu Yehova, khululukireni mphulupulu zanga, ngakhale kuti ndi zochuluka.
For thy name’s sake, O LORD, pardon mine iniquity, for it is great.
12 Tsono ndani munthu amene amaopa Yehova? Yehova adzamulangiza njira yoti ayitsate.
What man is he that feareth the LORD? him shall he instruct in the way that he shall choose.
13 Iye adzakhala pa ulemerero masiku ake onse, ndipo zidzukulu zake zidzalandira dziko ngati cholowa chawo.
His soul shall dwell at ease; and his seed shall inherit the land.
14 Yehova amawulula chinsinsi chake kwa iwo amene amamuopa; amawulula pangano lake kwa iwowo.
The secret of the LORD is with them that fear him; and he will shew them his covenant.
15 Maso anga ali pa Yehova nthawi zonse, pakuti ndi Iye yekha amene adzawonjola mapazi anga mu msampha.
Mine eyes are ever toward the LORD; for he shall pluck my feet out of the net.
16 Tembenukirani kwa ine ndipo mundikomere mtima, pakuti ndili ndekhandekha ndipo ndikuzunzika.
Turn thee unto me, and have mercy upon me; for I am desolate and afflicted.
17 Masautso a mu mtima mwanga achulukirachulukira; masuleni ku zowawa zanga.
The troubles of my heart are enlarged: O bring thou me out of my distresses.
18 Penyani mazunzo anga ndi zovuta zanga ndipo mufafanize machimo anga onse.
Consider mine affliction and my travail; and forgive all my sins.
19 Onani mmene adani anga achulukira ndi momwe chidani chawo ndi ine chakulira.
Consider mine enemies, for they are many; and they hate me with cruel hatred.
20 Tetezani moyo wanga ndi kundilanditsa; musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndimathawira kwa Inu.
O keep my soul, and deliver me: let me not be ashamed, for I put my trust in thee.
21 Kukhulupirika ndi kulungama kwanga kunditeteze, chifukwa chiyembekezo changa chili mwa Inu.
Let integrity and uprightness preserve me, for I wait on thee.
22 Wombolani Israeli Inu Mulungu, ku mavuto ake onse!
Redeem Israel, O God, out of all his troubles.

< Masalimo 25 >