< Masalimo 25 >
1 Salimo la Davide. Kwa Inu Yehova, ndipereka moyo wanga.
A Psalme of David. Unto thee, O Lord, lift I vp my soule.
2 Ndimadalira Inu Mulungu wanga. Musalole kuti ndichite manyazi kapena kuti adani anga andipambane.
My God, I trust in thee: let me not be confounded: let not mine enemies reioyce ouer mee.
3 Aliyense amene amayembekezera kwa Ambuye sadzachititsidwa manyazi koma achinyengo ndiwo adzachititsidwe manyazi ndipo sadzakhala ndi chodzitetezera.
So all that hope in thee, shall not be ashamed: but let them be confounded, that transgresse without cause.
4 Ndidziwitseni njira zanu Inu Yehova, phunzitseni mayendedwe anu;
Shew me thy waies, O Lord, and teache me thy paths.
5 tsogolereni mʼchoonadi chanu ndi kundiphunzitsa, pakuti Inu ndinu Mulungu mpulumutsi wanga, ndipo chiyembekezo changa chili mwa Inu tsiku lonse.
Leade me foorth in thy trueth, and teache me: for thou art the God of my saluation: in thee doe I trust all the day.
6 Kumbukirani Inu Yehova chifundo ndi chikondi chanu chachikulu, pakuti ndi zakalekale.
Remember, O Lord, thy tender mercies, and thy louing kindnesse: for they haue beene for euer.
7 Musakumbukire machimo a ubwana wanga ndi makhalidwe anga owukira; molingana ndi chikondi chanu ndikumbukireni ine, pakuti Inu Yehova ndinu wabwino.
Remember not the sinnes of my youth, nor my rebellions, but according to thy kindenesse remember thou me, euen for thy goodnesse sake, O Lord.
8 Yehova ndi wabwino ndi wolungama; choncho Iye akulangiza ochimwa mʼnjira yake.
Gracious and righteous is the Lord: therefore will he teache sinners in the way.
9 Amatsogolera odzichepetsa kuti achite zolungama ndipo amawaphunzitsa njira zake.
Them that be meeke, will hee guide in iudgement, and teach the humble his way.
10 Njira zonse za Yehova ndi zachikondi ndi zokhulupirika kwa iwo amene amasunga zofuna za pangano lake.
All the pathes of the Lord are mercie and trueth vnto such as keepe his couenant and his testimonies.
11 Chifukwa cha dzina lanu, Inu Yehova, khululukireni mphulupulu zanga, ngakhale kuti ndi zochuluka.
For thy Names sake, O Lord, be merciful vnto mine iniquitie, for it is great.
12 Tsono ndani munthu amene amaopa Yehova? Yehova adzamulangiza njira yoti ayitsate.
What man is he that feareth the Lord? him wil he teache the way that hee shall chuse.
13 Iye adzakhala pa ulemerero masiku ake onse, ndipo zidzukulu zake zidzalandira dziko ngati cholowa chawo.
His soule shall dwell at ease, and his seede shall inherite the land.
14 Yehova amawulula chinsinsi chake kwa iwo amene amamuopa; amawulula pangano lake kwa iwowo.
The secrete of the Lord is reueiled to them, that feare him: and his couenant to giue them vnderstanding.
15 Maso anga ali pa Yehova nthawi zonse, pakuti ndi Iye yekha amene adzawonjola mapazi anga mu msampha.
Mine eyes are euer towarde the Lord: for he will bring my feete out of the net.
16 Tembenukirani kwa ine ndipo mundikomere mtima, pakuti ndili ndekhandekha ndipo ndikuzunzika.
Turne thy face vnto mee, and haue mercie vpon me: for I am desolate and poore.
17 Masautso a mu mtima mwanga achulukirachulukira; masuleni ku zowawa zanga.
The sorowes of mine heart are enlarged: drawe me out of my troubles.
18 Penyani mazunzo anga ndi zovuta zanga ndipo mufafanize machimo anga onse.
Looke vpon mine affliction and my trauel, and forgiue all my sinnes.
19 Onani mmene adani anga achulukira ndi momwe chidani chawo ndi ine chakulira.
Beholde mine enemies, for they are manie, and they hate me with cruell hatred.
20 Tetezani moyo wanga ndi kundilanditsa; musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndimathawira kwa Inu.
Keepe my soule, and deliuer me: let me not be confounded, for I trust in thee.
21 Kukhulupirika ndi kulungama kwanga kunditeteze, chifukwa chiyembekezo changa chili mwa Inu.
Let mine vprightnes and equitie preserue me: for mine hope is in thee.
22 Wombolani Israeli Inu Mulungu, ku mavuto ake onse!
Deliuer Israel, O God, out of all his troubles.