< Masalimo 25 >
1 Salimo la Davide. Kwa Inu Yehova, ndipereka moyo wanga.
Of David. To you, O Lord, my soul is lifted up.
2 Ndimadalira Inu Mulungu wanga. Musalole kuti ndichite manyazi kapena kuti adani anga andipambane.
O my God, I have put my faith in you, let me not be shamed; let not my haters be glorying over me.
3 Aliyense amene amayembekezera kwa Ambuye sadzachititsidwa manyazi koma achinyengo ndiwo adzachititsidwe manyazi ndipo sadzakhala ndi chodzitetezera.
Let no servant of yours be put to shame; may those be shamed who are false without cause.
4 Ndidziwitseni njira zanu Inu Yehova, phunzitseni mayendedwe anu;
Make your steps clear to me, O Lord; give me knowledge of your ways.
5 tsogolereni mʼchoonadi chanu ndi kundiphunzitsa, pakuti Inu ndinu Mulungu mpulumutsi wanga, ndipo chiyembekezo changa chili mwa Inu tsiku lonse.
Be my guide and teacher in the true way; for you are the God of my salvation; I am waiting for your word all the day.
6 Kumbukirani Inu Yehova chifundo ndi chikondi chanu chachikulu, pakuti ndi zakalekale.
O Lord, keep in mind your pity and your mercies; for they have been from the earliest times.
7 Musakumbukire machimo a ubwana wanga ndi makhalidwe anga owukira; molingana ndi chikondi chanu ndikumbukireni ine, pakuti Inu Yehova ndinu wabwino.
Do not keep in mind my sins when I was young, or my wrongdoing: let your memory of me be full of mercy, O Lord, because of your righteousness.
8 Yehova ndi wabwino ndi wolungama; choncho Iye akulangiza ochimwa mʼnjira yake.
Good and upright is the Lord: so he will be the teacher of sinners in the way.
9 Amatsogolera odzichepetsa kuti achite zolungama ndipo amawaphunzitsa njira zake.
He will be an upright guide to the poor in spirit: he will make his way clear to them.
10 Njira zonse za Yehova ndi zachikondi ndi zokhulupirika kwa iwo amene amasunga zofuna za pangano lake.
All the ways of the Lord are mercy and good faith for those who keep his agreement and his witness.
11 Chifukwa cha dzina lanu, Inu Yehova, khululukireni mphulupulu zanga, ngakhale kuti ndi zochuluka.
Because of your name, O Lord, let me have forgiveness for my sin, which is very great.
12 Tsono ndani munthu amene amaopa Yehova? Yehova adzamulangiza njira yoti ayitsate.
If a man has the fear of the Lord, the Lord will be his teacher in the way of his pleasure.
13 Iye adzakhala pa ulemerero masiku ake onse, ndipo zidzukulu zake zidzalandira dziko ngati cholowa chawo.
His soul will be full of good things, and his seed will have the earth for its heritage.
14 Yehova amawulula chinsinsi chake kwa iwo amene amamuopa; amawulula pangano lake kwa iwowo.
The secret of the Lord is with those in whose hearts is the fear of him; he will make his agreement clear to them.
15 Maso anga ali pa Yehova nthawi zonse, pakuti ndi Iye yekha amene adzawonjola mapazi anga mu msampha.
My eyes are turned to the Lord at all times; for he will take my feet out of the net.
16 Tembenukirani kwa ine ndipo mundikomere mtima, pakuti ndili ndekhandekha ndipo ndikuzunzika.
Be turned to me, and have mercy on me; for I am troubled and have no helper.
17 Masautso a mu mtima mwanga achulukirachulukira; masuleni ku zowawa zanga.
The troubles of my heart are increased: O take me out of my sorrows.
18 Penyani mazunzo anga ndi zovuta zanga ndipo mufafanize machimo anga onse.
Give thought to my grief and my pain; and take away all my sins.
19 Onani mmene adani anga achulukira ndi momwe chidani chawo ndi ine chakulira.
See how those who are against me are increased, for bitter is their hate of me.
20 Tetezani moyo wanga ndi kundilanditsa; musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndimathawira kwa Inu.
O keep my soul, and take me out of danger: let me not be shamed, for I have put my faith in you.
21 Kukhulupirika ndi kulungama kwanga kunditeteze, chifukwa chiyembekezo changa chili mwa Inu.
For my clean and upright ways keep me safe, because my hope is in you.
22 Wombolani Israeli Inu Mulungu, ku mavuto ake onse!
Give Israel salvation, O God, out of all his troubles.