< Masalimo 25 >

1 Salimo la Davide. Kwa Inu Yehova, ndipereka moyo wanga.
大衛的詩。 耶和華啊,我的心仰望你。
2 Ndimadalira Inu Mulungu wanga. Musalole kuti ndichite manyazi kapena kuti adani anga andipambane.
我的上帝啊,我素來倚靠你; 求你不要叫我羞愧, 不要叫我的仇敵向我誇勝。
3 Aliyense amene amayembekezera kwa Ambuye sadzachititsidwa manyazi koma achinyengo ndiwo adzachititsidwe manyazi ndipo sadzakhala ndi chodzitetezera.
凡等候你的必不羞愧; 惟有那無故行奸詐的必要羞愧。
4 Ndidziwitseni njira zanu Inu Yehova, phunzitseni mayendedwe anu;
耶和華啊,求你將你的道指示我, 將你的路教訓我!
5 tsogolereni mʼchoonadi chanu ndi kundiphunzitsa, pakuti Inu ndinu Mulungu mpulumutsi wanga, ndipo chiyembekezo changa chili mwa Inu tsiku lonse.
求你以你的真理引導我,教訓我, 因為你是救我的上帝。 我終日等候你。
6 Kumbukirani Inu Yehova chifundo ndi chikondi chanu chachikulu, pakuti ndi zakalekale.
耶和華啊,求你記念你的憐憫和慈愛, 因為這是亙古以來所常有的。
7 Musakumbukire machimo a ubwana wanga ndi makhalidwe anga owukira; molingana ndi chikondi chanu ndikumbukireni ine, pakuti Inu Yehova ndinu wabwino.
求你不要記念我幼年的罪愆和我的過犯; 耶和華啊,求你因你的恩惠,按你的慈愛記念我。
8 Yehova ndi wabwino ndi wolungama; choncho Iye akulangiza ochimwa mʼnjira yake.
耶和華是良善正直的, 所以他必指示罪人走正路。
9 Amatsogolera odzichepetsa kuti achite zolungama ndipo amawaphunzitsa njira zake.
他必按公平引領謙卑人, 將他的道教訓他們。
10 Njira zonse za Yehova ndi zachikondi ndi zokhulupirika kwa iwo amene amasunga zofuna za pangano lake.
凡遵守他的約和他法度的人, 耶和華都以慈愛誠實待他。
11 Chifukwa cha dzina lanu, Inu Yehova, khululukireni mphulupulu zanga, ngakhale kuti ndi zochuluka.
耶和華啊,求你因你的名赦免我的罪, 因為我的罪重大。
12 Tsono ndani munthu amene amaopa Yehova? Yehova adzamulangiza njira yoti ayitsate.
誰敬畏耶和華, 耶和華必指示他當選擇的道路。
13 Iye adzakhala pa ulemerero masiku ake onse, ndipo zidzukulu zake zidzalandira dziko ngati cholowa chawo.
他必安然居住; 他的後裔必承受地土。
14 Yehova amawulula chinsinsi chake kwa iwo amene amamuopa; amawulula pangano lake kwa iwowo.
耶和華與敬畏他的人親密; 他必將自己的約指示他們。
15 Maso anga ali pa Yehova nthawi zonse, pakuti ndi Iye yekha amene adzawonjola mapazi anga mu msampha.
我的眼目時常仰望耶和華, 因為他必將我的腳從網裏拉出來。
16 Tembenukirani kwa ine ndipo mundikomere mtima, pakuti ndili ndekhandekha ndipo ndikuzunzika.
求你轉向我,憐恤我, 因為我是孤獨困苦。
17 Masautso a mu mtima mwanga achulukirachulukira; masuleni ku zowawa zanga.
我心裏的愁苦甚多, 求你救我脫離我的禍患。
18 Penyani mazunzo anga ndi zovuta zanga ndipo mufafanize machimo anga onse.
求你看顧我的困苦,我的艱難, 赦免我一切的罪。
19 Onani mmene adani anga achulukira ndi momwe chidani chawo ndi ine chakulira.
求你察看我的仇敵, 因為他們人多,並且痛痛地恨我。
20 Tetezani moyo wanga ndi kundilanditsa; musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndimathawira kwa Inu.
求你保護我的性命,搭救我, 使我不致羞愧,因為我投靠你。
21 Kukhulupirika ndi kulungama kwanga kunditeteze, chifukwa chiyembekezo changa chili mwa Inu.
願純全、正直保守我, 因為我等候你。
22 Wombolani Israeli Inu Mulungu, ku mavuto ake onse!
上帝啊,求你救贖以色列脫離他一切的愁苦。

< Masalimo 25 >