< Masalimo 25 >

1 Salimo la Davide. Kwa Inu Yehova, ndipereka moyo wanga.
【靠上主的祈禱】上主,我向你把我的心舉起,
2 Ndimadalira Inu Mulungu wanga. Musalole kuti ndichite manyazi kapena kuti adani anga andipambane.
我的天主,我全心要倚靠你。求你不要使我蒙受羞恥,不要容許我的仇人歡喜。
3 Aliyense amene amayembekezera kwa Ambuye sadzachititsidwa manyazi koma achinyengo ndiwo adzachititsidwe manyazi ndipo sadzakhala ndi chodzitetezera.
凡期望你的人絕不會蒙羞,唯冒昧失信人才會受辱。
4 Ndidziwitseni njira zanu Inu Yehova, phunzitseni mayendedwe anu;
上主,求你使我認識你的法度,並求你教訓我履行你的道路。
5 tsogolereni mʼchoonadi chanu ndi kundiphunzitsa, pakuti Inu ndinu Mulungu mpulumutsi wanga, ndipo chiyembekezo changa chili mwa Inu tsiku lonse.
還求你教訓我;引我進入真理之路,我終日仰望你,因你是救我的天主。
6 Kumbukirani Inu Yehova chifundo ndi chikondi chanu chachikulu, pakuti ndi zakalekale.
上主,求你憶及的仁慈和恩愛,因為它們由亙古以來就常存在。
7 Musakumbukire machimo a ubwana wanga ndi makhalidwe anga owukira; molingana ndi chikondi chanu ndikumbukireni ine, pakuti Inu Yehova ndinu wabwino.
我青春的罪愆和過犯,求你要追念;上主,求你紀念我,照你的仁慈和良善。
8 Yehova ndi wabwino ndi wolungama; choncho Iye akulangiza ochimwa mʼnjira yake.
因為上主仁慈又正直,常領迷途者歸回正路,
9 Amatsogolera odzichepetsa kuti achite zolungama ndipo amawaphunzitsa njira zake.
引導謙卑者遵守正義,教善良者走入正途。
10 Njira zonse za Yehova ndi zachikondi ndi zokhulupirika kwa iwo amene amasunga zofuna za pangano lake.
對待持守上主的盟約和誡命的人,上主的一切行徑常是慈愛和忠誠。
11 Chifukwa cha dzina lanu, Inu Yehova, khululukireni mphulupulu zanga, ngakhale kuti ndi zochuluka.
上主,為了你聖名的緣故,求你赦免我重大的愆尤。
12 Tsono ndani munthu amene amaopa Yehova? Yehova adzamulangiza njira yoti ayitsate.
不論是誰,只要他敬愛上主,上主必指示他應選的道路,
13 Iye adzakhala pa ulemerero masiku ake onse, ndipo zidzukulu zake zidzalandira dziko ngati cholowa chawo.
他的心靈必要安享幸福,他的後裔必能承繼領土。
14 Yehova amawulula chinsinsi chake kwa iwo amene amamuopa; amawulula pangano lake kwa iwowo.
上主親近敬愛自己的人民,也使他們認識自己的誓盟。
15 Maso anga ali pa Yehova nthawi zonse, pakuti ndi Iye yekha amene adzawonjola mapazi anga mu msampha.
我的眼睛不斷地向上主瞻仰,因為祂使我的雙腳脫離羅網。
16 Tembenukirani kwa ine ndipo mundikomere mtima, pakuti ndili ndekhandekha ndipo ndikuzunzika.
求你回顧,求你憐憫,因為我是孤苦伶仃。
17 Masautso a mu mtima mwanga achulukirachulukira; masuleni ku zowawa zanga.
求你減輕我心的苦難,救我脫離我的憂患;
18 Penyani mazunzo anga ndi zovuta zanga ndipo mufafanize machimo anga onse.
垂視我的勞苦和可憐,赦免我犯的一切罪愆。
19 Onani mmene adani anga achulukira ndi momwe chidani chawo ndi ine chakulira.
請看我的仇敵如何眾多,他們都兇狠地痛恨著我。
20 Tetezani moyo wanga ndi kundilanditsa; musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndimathawira kwa Inu.
求你保謢我的生命,向我施救,別叫我因投奔你而蒙受羞辱。
21 Kukhulupirika ndi kulungama kwanga kunditeteze, chifukwa chiyembekezo changa chili mwa Inu.
願清白和正直護衛我!上主,因我唯有仰望你。
22 Wombolani Israeli Inu Mulungu, ku mavuto ake onse!
天主,求你拯救以色列,使他脫離一切的禍災

< Masalimo 25 >