< Masalimo 24 >
1 Salimo la Davide. Dziko lapansi ndi la Yehova ndi zonse zimene zili mʼmenemo, dziko ndi onse amene amakhala mʼmenemo;
De Yavé es la tierra y lo que hay en ella, El mundo y los que habitan en él.
2 pakuti Iye ndiye anayika maziko ake pa nyanja ndi kulikhazika pamwamba pa madzi.
Porque Él la fundó sobre los mares Y la afirmó sobre las corrientes de agua.
3 Ndani angakwere phiri la Yehova? Ndani angathe kuyima pa malo ake opatulika?
¿Quién subirá a la Montaña de Yavé? ¿Quién podrá estar en pie en su Santuario?
4 Iye amene ali ndi mʼmanja moyera ndi mtima woyera, amene sapereka moyo wake kwa fano kapena kulumbira mwachinyengo.
El limpio de manos y puro de corazón, El que no elevó su alma a la falsedad Ni juró con engaño.
5 Iyeyo adzalandira madalitso kwa Yehova ndipo Mulungu mpulumutsi wake adzagamula kuti alibe mlandu.
Él recibirá bendición de Yavé Y la justicia del ʼElohim de su salvación.
6 Umenewo ndiwo mʼbado wa amene amafunafuna Yehova; amene amafunafuna nkhope yanu, Inu Mulungu wa Yakobo. (Sela)
Esta es la generación de los que lo buscan, De los que buscan tu rostro, [oh] ʼElohim de Jacob. (Selah)
7 Tukulani mitu yanu inu zipata; tsekukani, inu zitseko zakalekalenu, kuti Mfumu yaulemerero ilowe.
¡Alcen, oh puertas, sus cabezas! ¡Sean levantados, portales eternos, Y entrará el Rey de gloria!
8 Kodi Mfumu yaulemereroyo ndani? Yehova Wamphamvuzonse, Yehova ndiye wamphamvu pa nkhondo.
¿Quién es este Rey de gloria? ¡Yavé, el Fuerte y Poderoso! ¡Yavé, el Poderoso en batalla!
9 Tukulani mitu yanu, inu zipata; tsekukani, inu zitseko zakalekalenu, kuti Mfumu yaulemerero ilowe.
¡Alcen, oh puertas, sus cabezas! ¡Sean levantados, portales eternos, Y entrará el Rey de gloria!
10 Kodi Mfumu yaulemereroyo ndani? Yehova Wamphamvuzonse, Iye ndiye Mfumu yaulemerero. (Sela)
¿Quién es este Rey de gloria? ¡Yavé de las huestes! ¡Él es el Rey de gloria! (Selah)