< Masalimo 24 >

1 Salimo la Davide. Dziko lapansi ndi la Yehova ndi zonse zimene zili mʼmenemo, dziko ndi onse amene amakhala mʼmenemo;
Salmo de Davi: Ao SENHOR [pertence] a terra, e sua plenitude; o mundo, e os que nele habitam.
2 pakuti Iye ndiye anayika maziko ake pa nyanja ndi kulikhazika pamwamba pa madzi.
Porque ele a fundou sobre os mares; e sobre os rios ele a firmou.
3 Ndani angakwere phiri la Yehova? Ndani angathe kuyima pa malo ake opatulika?
Quem subirá ao monte do SENHOR? E quem ficará de pé no lugar de sua santidade?
4 Iye amene ali ndi mʼmanja moyera ndi mtima woyera, amene sapereka moyo wake kwa fano kapena kulumbira mwachinyengo.
Aquele que é limpo de mãos, e puro de coração, que não entrega sua alma para as coisas vãs, nem jura enganosamente.
5 Iyeyo adzalandira madalitso kwa Yehova ndipo Mulungu mpulumutsi wake adzagamula kuti alibe mlandu.
Este receberá a bênção do SENHOR, e a justiça do Deus de sua salvação.
6 Umenewo ndiwo mʼbado wa amene amafunafuna Yehova; amene amafunafuna nkhope yanu, Inu Mulungu wa Yakobo. (Sela)
Esta é a geração dos que o buscam, dos que procuram a tua face: [a geração de] Jacó. (Selá)
7 Tukulani mitu yanu inu zipata; tsekukani, inu zitseko zakalekalenu, kuti Mfumu yaulemerero ilowe.
Levantai, portas, vossas cabeças; e levantai-vos vós, entradas eternas; para que entre o Rei da Glória.
8 Kodi Mfumu yaulemereroyo ndani? Yehova Wamphamvuzonse, Yehova ndiye wamphamvu pa nkhondo.
Quem é o Rei da Glória? O SENHOR forte e poderoso, o SENHOR poderoso na guerra.
9 Tukulani mitu yanu, inu zipata; tsekukani, inu zitseko zakalekalenu, kuti Mfumu yaulemerero ilowe.
Levantai, portas, vossas cabeças; e levantai-vos vós, entradas eternas; para que entre o Rei da Glória.
10 Kodi Mfumu yaulemereroyo ndani? Yehova Wamphamvuzonse, Iye ndiye Mfumu yaulemerero. (Sela)
Quem é este Rei da Glória? O SENHOR dos exércitos; ele é o Rei da Glória! (Selá)

< Masalimo 24 >