< Masalimo 24 >
1 Salimo la Davide. Dziko lapansi ndi la Yehova ndi zonse zimene zili mʼmenemo, dziko ndi onse amene amakhala mʼmenemo;
Psalm Dawida. Do PANA należy ziemia i wszystko, co ją napełnia, świat i jego mieszkańcy.
2 pakuti Iye ndiye anayika maziko ake pa nyanja ndi kulikhazika pamwamba pa madzi.
Na morzach bowiem ugruntował go i utwierdził na rzekach.
3 Ndani angakwere phiri la Yehova? Ndani angathe kuyima pa malo ake opatulika?
Któż wstąpi na górę PANA? Kto stanie w jego świętym miejscu?
4 Iye amene ali ndi mʼmanja moyera ndi mtima woyera, amene sapereka moyo wake kwa fano kapena kulumbira mwachinyengo.
[Człowiek] rąk nieskalanych i czystego serca, który nie skłania swej duszy ku marności i nie przysięga podstępnie.
5 Iyeyo adzalandira madalitso kwa Yehova ndipo Mulungu mpulumutsi wake adzagamula kuti alibe mlandu.
On otrzyma błogosławieństwo od PANA i sprawiedliwość od Boga, swego Zbawiciela.
6 Umenewo ndiwo mʼbado wa amene amafunafuna Yehova; amene amafunafuna nkhope yanu, Inu Mulungu wa Yakobo. (Sela)
To jest pokolenie tych, którzy go szukają, którzy szukają twego oblicza, [Boże] Jakuba. (Sela)
7 Tukulani mitu yanu inu zipata; tsekukani, inu zitseko zakalekalenu, kuti Mfumu yaulemerero ilowe.
Podnieście, o bramy, wasze głowy; podnieście się, wrota odwieczne, aby wszedł Król chwały.
8 Kodi Mfumu yaulemereroyo ndani? Yehova Wamphamvuzonse, Yehova ndiye wamphamvu pa nkhondo.
Któż jest tym Królem chwały? PAN mocny i potężny, PAN potężny w boju.
9 Tukulani mitu yanu, inu zipata; tsekukani, inu zitseko zakalekalenu, kuti Mfumu yaulemerero ilowe.
Podnieście, o bramy, wasze głowy; podnieście się, wrota odwieczne, aby wszedł Król chwały.
10 Kodi Mfumu yaulemereroyo ndani? Yehova Wamphamvuzonse, Iye ndiye Mfumu yaulemerero. (Sela)
Któż jest tym Królem chwały? PAN zastępów, on [jest] Królem chwały. (Sela)