< Masalimo 24 >
1 Salimo la Davide. Dziko lapansi ndi la Yehova ndi zonse zimene zili mʼmenemo, dziko ndi onse amene amakhala mʼmenemo;
SAPWILIM en Ieowa sappa o audepa kan, sap o meakaros me kauson poa.
2 pakuti Iye ndiye anayika maziko ake pa nyanja ndi kulikhazika pamwamba pa madzi.
Pwe a kotin pasonedier ni kailan madau, o a kotin wiadar pon pil akan.
3 Ndani angakwere phiri la Yehova? Ndani angathe kuyima pa malo ake opatulika?
Is me pan kodalang pon dol en Ieowa? O is me pan kak uda ni mol en Ieowa saraui?
4 Iye amene ali ndi mʼmanja moyera ndi mtima woyera, amene sapereka moyo wake kwa fano kapena kulumbira mwachinyengo.
Me pa a kan sota sapung o mongiong i makelekel; me sota kin mauki padak sapung, o me sota kin kaula likam.
5 Iyeyo adzalandira madalitso kwa Yehova ndipo Mulungu mpulumutsi wake adzagamula kuti alibe mlandu.
I me pan kamaula ren Ieowa, o a pan pung kila ren Kot a saunkamaur.
6 Umenewo ndiwo mʼbado wa amene amafunafuna Yehova; amene amafunafuna nkhope yanu, Inu Mulungu wa Yakobo. (Sela)
I kainok, me kin peiki ong Kot, me kin rapaki silang omui, Kot en Iakop. (Sela)
7 Tukulani mitu yanu inu zipata; tsekukani, inu zitseko zakalekalenu, kuti Mfumu yaulemerero ilowe.
Komail ritingada wanim laud o langada wanim nin sappa, pwe Nammarki lingan en kotilong!
8 Kodi Mfumu yaulemereroyo ndani? Yehova Wamphamvuzonse, Yehova ndiye wamphamvu pa nkhondo.
Is Nanmarki lingan men et? I Ieowa roson o manaman, Ieowa me rasong nan mauin.
9 Tukulani mitu yanu, inu zipata; tsekukani, inu zitseko zakalekalenu, kuti Mfumu yaulemerero ilowe.
Komail ritingada wanim laud o langada wanim nin sappa, pwe Nanmarki lingan en kotilong!
10 Kodi Mfumu yaulemereroyo ndani? Yehova Wamphamvuzonse, Iye ndiye Mfumu yaulemerero. (Sela)
Is Nanmarki lingan men et? I Ieowa Sepaot; I Nanmarki lingan. (Sela)