< Masalimo 24 >

1 Salimo la Davide. Dziko lapansi ndi la Yehova ndi zonse zimene zili mʼmenemo, dziko ndi onse amene amakhala mʼmenemo;
Prima sabbati. Psalmus David. [Domini est terra, et plenitudo ejus; orbis terrarum, et universi qui habitant in eo.
2 pakuti Iye ndiye anayika maziko ake pa nyanja ndi kulikhazika pamwamba pa madzi.
Quia ipse super maria fundavit eum, et super flumina præparavit eum.
3 Ndani angakwere phiri la Yehova? Ndani angathe kuyima pa malo ake opatulika?
Quis ascendet in montem Domini? aut quis stabit in loco sancto ejus?
4 Iye amene ali ndi mʼmanja moyera ndi mtima woyera, amene sapereka moyo wake kwa fano kapena kulumbira mwachinyengo.
Innocens manibus et mundo corde, qui non accepit in vano animam suam, nec juravit in dolo proximo suo:
5 Iyeyo adzalandira madalitso kwa Yehova ndipo Mulungu mpulumutsi wake adzagamula kuti alibe mlandu.
hic accipiet benedictionem a Domino, et misericordiam a Deo salutari suo.
6 Umenewo ndiwo mʼbado wa amene amafunafuna Yehova; amene amafunafuna nkhope yanu, Inu Mulungu wa Yakobo. (Sela)
Hæc est generatio quærentium eum, quærentium faciem Dei Jacob.
7 Tukulani mitu yanu inu zipata; tsekukani, inu zitseko zakalekalenu, kuti Mfumu yaulemerero ilowe.
Attollite portas, principes, vestras, et elevamini, portæ æternales, et introibit rex gloriæ.
8 Kodi Mfumu yaulemereroyo ndani? Yehova Wamphamvuzonse, Yehova ndiye wamphamvu pa nkhondo.
Quis est iste rex gloriæ? Dominus fortis et potens, Dominus potens in prælio.
9 Tukulani mitu yanu, inu zipata; tsekukani, inu zitseko zakalekalenu, kuti Mfumu yaulemerero ilowe.
Attollite portas, principes, vestras, et elevamini, portæ æternales, et introibit rex gloriæ.
10 Kodi Mfumu yaulemereroyo ndani? Yehova Wamphamvuzonse, Iye ndiye Mfumu yaulemerero. (Sela)
Quis est iste rex gloriæ? Dominus virtutum ipse est rex gloriæ.]

< Masalimo 24 >