< Masalimo 24 >

1 Salimo la Davide. Dziko lapansi ndi la Yehova ndi zonse zimene zili mʼmenemo, dziko ndi onse amene amakhala mʼmenemo;
Psaume de David, pour le premier jour de la semaine. La terre est au Seigneur, et tout ce qu'elle contient, le monde et ceux qui l'habitent.
2 pakuti Iye ndiye anayika maziko ake pa nyanja ndi kulikhazika pamwamba pa madzi.
Il l'a fondée sur la mer, il l'a préparée sur les fleuves.
3 Ndani angakwere phiri la Yehova? Ndani angathe kuyima pa malo ake opatulika?
Qui montera sur la montagne du Seigneur? qui se tiendra dans son sanctuaire?
4 Iye amene ali ndi mʼmanja moyera ndi mtima woyera, amene sapereka moyo wake kwa fano kapena kulumbira mwachinyengo.
Celui dont les mains sont innocentes et dont le cœur est pur; qui n'a point reçu en vain son âme; qui n'a point trompé son prochain par de faux serments.
5 Iyeyo adzalandira madalitso kwa Yehova ndipo Mulungu mpulumutsi wake adzagamula kuti alibe mlandu.
Celui-là recevra la bénédiction du Seigneur, et la miséricorde de Dieu son Sauveur.
6 Umenewo ndiwo mʼbado wa amene amafunafuna Yehova; amene amafunafuna nkhope yanu, Inu Mulungu wa Yakobo. (Sela)
Telle est la génération de ceux qui le cherchent, qui cherchent la face du Dieu de Jacob. Interlude.
7 Tukulani mitu yanu inu zipata; tsekukani, inu zitseko zakalekalenu, kuti Mfumu yaulemerero ilowe.
Princes, levez vos portes; ouvrez-vous, portes éternelles, et le Roi de gloire entrera.
8 Kodi Mfumu yaulemereroyo ndani? Yehova Wamphamvuzonse, Yehova ndiye wamphamvu pa nkhondo.
Quel est donc le Roi de gloire? C'est le Seigneur fort et puissant, le Seigneur puissant au combat.
9 Tukulani mitu yanu, inu zipata; tsekukani, inu zitseko zakalekalenu, kuti Mfumu yaulemerero ilowe.
Princes, levez vos portes; ouvrez-vous, portes éternelles, et le Roi de gloire entrera.
10 Kodi Mfumu yaulemereroyo ndani? Yehova Wamphamvuzonse, Iye ndiye Mfumu yaulemerero. (Sela)
Quel est donc ce Roi de gloire? C'est le Dieu des vertus, c'est lui qui est le Roi de gloire.

< Masalimo 24 >