< Masalimo 23 >
1 Salimo la Davide. Yehova ndiye mʼbusa wanga, sindidzasowa kanthu.
Psaume de David.
2 Amandigoneka pa msipu wobiriwira, amanditsogolera ku madzi akumwa abwino,
C’est dans un lieu de pâture qu’il m’a placé. C’est auprès d’une eau fortifiante qu’il m’a élevé.
3 amatsitsimutsa moyo wanga. Amanditsogolera mʼnjira zachilungamo chifukwa cha dzina lake.
Il a fait revenir mon âme. Il m’a conduit dans les sentiers de la justice, à cause de son nom.
4 Ngakhale ndiyende mʼchigwa cha mdima wakuda bii, sindidzaopa choyipa, pakuti Inu muli ndi ine; chibonga chanu ndi ndodo yanu zimanditonthoza.
Car quand je marcherais au milieu de l’ombre de la mort, je ne craindrais point les maux, parce que vous êtes avec moi. Votre verge et votre bâton m’ont consolé.
5 Mumandikonzera chakudya adani anga akuona. Mumadzoza mutu wanga ndi mafuta; chikho changa chimasefukira.
Vous avez préparé en ma présence une table, en face de ceux qui me tourmentent. Vous avez oint ma tête d’huile; et mon calice enivrant, combien il est magnifique!
6 Zoonadi, zokoma ndi chikondi chosasinthika zidzanditsata masiku onse a moyo wanga, ndipo ndidzakhala mʼNyumba ya Yehova kwamuyaya.
Et votre miséricorde me suivra tous les jours de ma vie, Afin que j’habite dans la maison du Seigneur durant de longs jours.